Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Hoseya 6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Israyeli abwerera kunka kwa Yehova

1. Tiyeni, tibwerere kunka kwa Yehova; pakuti wang'amba, nadzatipoletsera; wakantha, nadzatimanga.

2. Atapita masiku awiri adzatitsitsimutsa, tsiku lacitatu adzatiutsa; ndipo tidzakhala ndi moyo pamaso pace.

3. Tidziwe tsono, tilondole kudziwa Yehova; kuturuka kwace kwakonzekeratu ngati matanda kuca; ndipo adzatidzera ngati mvula, ngati mvula ya masika yakuthirira dziko.

Efraimu ndi Yuda adrudzulidwa

4. Efraimu iwe, ndidzakucitira ciani? Yuda iwe, ndikucitire ciani? pakuti kukoma mtima kwako kukunga mtambo wam'mawa ndi ngati mame akuphawa mamawa.

5. Cifukwa cace ndawalikha mwa aneneri; ndawapha ndi mau a pakamwa panga; ndi maweruzo anga aturuka ngati kuunika.

6. Pakuti ndikondwera naco cifundo, si nsembe ai; ndi kumdziwa Mulungu koposa nsembe zopsereza.

7. Koma iwo analakwira cipangano ngati Adamu, m'mene anandicitira monyenga.

8. Gileadi ndiwo mudzi wa ocita zoipa, wa mapazi a mwazi.

9. Ndipo monga magulu a mbala alalira munthu, momwemo msonkhano wa ansembe amapha pa njira ya ku Sekemu; indedi acita coipitsitsa.

10. M'nyumba ya Israyeli ndinaona cinthu coopsetsa; pamenepo pali citole ca Efraimu; Israyeli wadetsedwa.

11. Akuikidwiratunso nyengo yakukolola, Yuda iwe, pamene ndikabwezanso undende wa anthu anga.