1. Lipenga kukamwa kwako, Akudza ngati ciombankhanga, kulim bana ndi nyumba ya Yehova; cifukwa analakwira cipangano canga, napikisana naco cilamulo canga.
2. Adzapfuulira kwa Ine, Mulungu wanga, ife Aisrayeli tikudziwani.
3. Israyeli wacitaya cokoma, mdani adzamlondola.
4. Analonga mafumu, koma sikunacokera kwa Ine; anaika akalonga, koma sindinadziwa; anadzipangira mafano a siliva wao ndi golidi wao, kuti akalikhidwe.
5. Mwana wa ng'ombe wako wakutaya, Samariya iwe; mkwiyo wanga wayakira iwo; adzalephera kuyera mtima mpaka liti?
6. Pakuti ici comwe cafumira kwa Israyeli; mmisiri wampanga, koma sali Mulungu; inde mwana wa ng'ombe wa Samariya adzaphwanyika-phwanyika.
7. Pakuti abzala mphepo, nadzakolola kabvumvulu; alibe tirigu wosasenga; ngala siidzaturutsa ufa; cinkana iuturutsa, alendo adzaumeza.
8. Israyeli wamezedwa; tsopano ali mwa amitundu ngati cotengera coti munthu sakondwera naco.
9. Pakuti anakwera kumka ku Asuri, ngati mbidzi ya pa yokha mwini wace; Efraimu walembera omkonda ngati anchito.
10. Inde angakhale alembera mwa amitundu ndidzawasonkhanitsa tsopano; ndipo ayamba kucepa cifukwa ca katundu wa mfumu ya akalonga.
11. Popeza Efraimu anacurukitsa maguwa a nsembe akucimwako, maguwa a nsembe omwewo anamcimwitsa.
12. Ndinamlembera zinthu zambirimbirizo za cilamulo canga, koma zinayesedwa ngati cinthu cacilendo.
13. Kunena za nsembe za zopereka zanga, aphera nsembe yanyama, naidya; koma Yehova sazilandira; tsopano adzakumbukila mphulupulu yao, nadzalanga zocimwa zao; adzabwerera kumka ku Aigupto.
14. Pakuti Israyeli waiwala Mlengi wace, namanga akacisit ndipo Yuda wacurukitsa midzi yamalinga; koma ndidzatumizira midzi yace moto, nudzatha nyumba zace zazikuru.