Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 17:14-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo mwamuna wosadulidwa, wosadulidwa khungu lace munthuyo amsadze mwa anthu a mtundu wace; waphwanya pangano langa.

15. Ndipo Mulungu anati kwa Abrahamu, Koma Sarai mkazi wako, usamcha dzina lace Sarai, koma dzina lace ndi Sara.

16. Ndipo ndidzamdalitsa iye, ndiponso ndidzakupatsa iwe mwana wamwamuna wobadwa mwa iye, inde, ndidzamdalitsa iye, ndipo adzakhala amace a mitundu, mafumu a anthu adzaturuka mwa iye.

17. Ndipo Abrahamu adagwa nkhope pansi, naseka, nati m'mtima mwace, Kodi mwana adzabadwa kwa iye amene ali wa zaka zana? Kodi Sara wa zaka makumi asanu ndi anai adzabala?

18. Ndipo Abrahamu anati kwa Mulungu, Ha! Ismayeli akhale ndi moyo pamaso panu!

19. Ndipo Mulungu anati, Koma Sara mkazi wako adzakubalira iwe mwana wamwamuna; ndipo udzamucha dzina lace Isake; ndipo ndidzalimbikitsa nave pangano langa, kuti likhale pangano la nthawi zonse, la ku mbeu zace za pambuyo pace.

20. Koma za Ismayeli, ndamvera iwe: taona, ndamdalitsa iye, ndipo ndidzamcurukitsa iye ndithu; adzabala akaronga khumi ndi awiri, ndipo ndidzamuyesa iye mtundu waukuru.

21. Koma pangano langa ndidzalimbikitsa ndi Isake, amene Sara adzakubalira iwe nthawi yomwe yino caka camawa.

22. Ndipo analeka kunena naye, ndipo Mulungu anakwera kucokera kwa Abrahamu.

Werengani mutu wathunthu Genesis 17