Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 7:1-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali pakukhala mfumuyo m'nyumba mwace, atampumulitsa Yehova pa adani ace onse omzungulira,

2. mfumuyo inanena ndi Natani mneneriyo, Onani ndirikukhala ine m'nyumba yamikungudza, koma likasa la Mulungu liri m'kati mwa nsaru zocinga.

3. Ndipo Natani anati kwa mfumuyo, Mukani mucite conse ciri mumtima mwanu, pakuti Yehova ali nanu,

4. Ndipo kunali usiku womwewo mau a Yehova anafika kwa Natani, kuti,

5. Kauze mtumiki wanga Davide, kuti, Atero Yehova, Kodi iwe udzandimangira nyumba yakuti ndikhalemo Ine?

6. pakuti sindinakhala m'nyumba kuyambira tsiku lija ndinaturutsa ana a Israyeli ku Aigupto kufikira lero lomwe, kama ndinayenda m'cihema ndi m'nyumba wamba.

7. M'malo monse ndinayendamo limodzi ndi ana onse a Israyeli kodi ndinanena ndi pfuko limodzi la Aisrayeli, limene ndinalamulira kudyetsa anthu anga Aisrayeli, kuti, Munalekeranji kundimangira nyumba yamikungudza?

8. Cifukwa cace tsono udzatero kwa mtumiki wanga Davide, Atero Yehova wa makamu, Ndinakucotsa kubusako kumene unalikutsata nkhosa kuti udzakhale mfumu ya anthu anga, ndiwo Israyeli,

9. Ndipo ndinali nawe kuli konse unamukako, ndi kuononga adani ako onse pamaso pako; ndipo ndidzamveketsa dzina lako, monga dzina la akuru ali pa dziko lapansi,

10. Ndipo ndidzaikira anthu anga Israyeli malo, ndi kuwaoka kuti akakhale m'malo ao a iwo okha, osasunthikanso. Ndipo anthu a mphulupulu sadzawabvutanso, monga poyamba paja,

11. monga kuyambira tsiku lija ndinalamulira oweruza kuyang'anira anthu anga Israyeli; ndipo ndidzakupumulitsa kwa adani ako onse. Yehova akuuzanso kuti Yehova adzakumangira banja.

12. Pamene masiku ako akadzakwaniridwa, ndipo iwe udzagona ndi makolo ako, Ine ndidzaukitsa mbeu yako pambuyo pako, imene idzaturuka m'matumbo mwako, ndipo ndidzakhazikitsa ufumu wace.

13. Iye adzamangira dzina langa nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa cimpando ca ufumu wace ku nthawi zonse.

14. Ndidzakhala atate wace, iye nadzakhala mwana wanga; akacita coipa ndidzamlanga ndi ndodo ya anthu, ndi mikwapulo ya ana a anthu;

15. koma cifundo canga sicidzamcokera iye, monga ndinacicotsera Sauli amene ndinamcotsa pamaso pako.

16. Ndipo nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhazikikadi ku nthawi zonse pamaso pako; mpando wacifumu wako udzakhazikika ku nthawi zonse.

17. Monga mwa mau onse awa ndi monga mwa masomphenya onse awa, momwemo Natani analankhula ndi Davide.

18. Pomwepo Davide mfumu analowa, nakhalapansi pamaso pa Yehova; nati, Ine ndine yani, Yehova Mulungu, ndi banja langa ndi ciani kuti munandifikitsa pano?

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 7