Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 20:1-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kudangotero kuti pamenepo panali munthu woipa, dzina lace ndiye Seba mwana wa Bikri Mbenjamini; naliza iye lipenga, nati, Ife tiribe gawo mwa Davide, tiribenso colowa mwa mwana wa Jese; munthu yense apite ku mahema ace, Israyeli inu.

2. Comweco anthu onse a Israyeli analeka kutsata Davide, natsata Seba mwana wa Bikri; koma anthu a Yuda anaphatikizana ndi mfumu yao, kuyambira ku Yordano kufikira ku Yerusalemu.

3. Ndipo Davide anafika kunyumba kwace ku Yerusalemu. Mfumuyo nitenga akazi khumi ang'onowo amene adawasiya asunge nyumbayo, nawatsekera m'nyumba, nawapatsa cakudya, koma sanalowana nao. Comweco iwowa anatsekedwa kufikira tsiku la imfa yao, nakhala ngati akazi amasiye.

4. Pamenepo mfumu inati kwa Amasa, Undiitanire anthu a Yuda asonkhane asanapite masiku atatu, nukhale pano iwenso.

5. Comweco Amasa anamuka kukaitana anthu a Yuda asonkhane; koma anacedwa, napitiriza nthawi imene idamuikira.

6. Ndipo Davide anati kwa Abisai, Tsopano Seba mwana wa Bikri adzaticitira coipa coposa cija ca Abisalomu; utenge anyamata a mbuye wako numtsatire, kuti angapeze midzi ya malinga ndi kupulumuka osaonekanso.

7. Ndipo anaturuka namtsata anthu a Yoabu, ndi Akereti ndi Apeleti, ndi anthu onseamphamvu; naturuka m'Yerusalemu kukalondola Seba mwana wa Bikri.

8. Pamene anafika iwo pa mwala waukuru uli ku Gibeoni, Amasa anadza kukomana nao. Ndipo Yoabu atabvala mwinjiro wace, anadzimangirira lamba lolongamo lupanga m'cimace m'cuuno mwace; ndipo m'kuyenda kwace lidasololoka.

9. Ndipo Yoabu ananena ndi Amasa, Uli bwino mbale wanga? Ndipo Yoabu anagwira ndebvu za Amasa ndi dzanja lace lamanja kuti ampsompsone.

10. Koma Amasa sanasamalira lupanga liri m'dzanja la Yoabu; comweco iye anamgwaza nalo m'mimba; nakhuthula matumbo ace pansi, osamgwazanso; nafa iye, Ndipo Yoabu ndi Abisai mbale wace analondola Seba mwana wa Bikri.

11. Ndipo mnyamata wina wa Yoabu anaima pali iye, nati, Wobvomereza Yoabu, ndi iye amene ali wace wa Davide, atsate Yoabu.

12. Ndipo Amasa analikukunkhulira m'mwazi wace pakati pa mseu. Ndipo pamene munthuyo anaona kuti anthu onse anaima, iye ananyamula Amasa namcotsa pamseu kumka naye kuthengo, nampfunda ndi cobvala, pamene anaona kuti anaima munthu yense wakufika pali iye.

13. Atamcotsa iye mumseu, anthu onse anapitirira kumsata Yoabu kukalondola Seba mwana wa Bikri.

14. Ndipo anapyola mapfuko onse a Israyeli kufikira ku Abeli ndi ku Betimaaka, ndi kwa Aberi onse; iwo nasonkhana pamodzi namlondolanso.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 20