Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 14:34-49 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

34. Ndipo Sauli anati, Balalikani pakati pa anthu, nimuwauze kuti abwere kwa ine kuno munthu yense ndi ng'ombe yace, ndi munthu yense ndi nkhosa yace, aziphe pano, ndi kuzidya, osacimwira Yehova ndi kudya zamwazi. Nabwera anthu onse, yense ndi ng'ombe yace, usiku uja naziphera pomwepo.

35. Ndipo Sauli anamangira Yehova guwa la nsembe; limenelo ndilo guwa loyamba iye anamangira Yehova.

36. Ndipo Sauli anati, Tiyeni titsikire usiku kwa Afilistiwo, ndi kuwawawanya kufikira kutayera, tisasiye munthu mmodzi wa iwowa. Ndipo iwo anati, Citani ciri conse cikukomerani. Pamenepo wansembeyo anati, Tisendere kwa Yehova kuno.

37. Ndipo Sauli anafunsira uphungu kwa Mulungu, Nditsikire kodi kwa Afilisti? Mudzawapereka m'dzanja la Israyeli kodi? Koma iye sanamyankha tsiku lomweli.

38. Ndipo Sauli anati, Musendere kuno, inu nonse akuru a anthu; kuti muzindikire ndi kuona m'mene muli coipa ici lero.

39. Pakuti, pali Yehova wakupulumutsa Israyeli, cingakhale ciri m'mwana wanga Jonatani, koma adzafa ndithu. Koma pakati pa anthu onse panalibe mmodzi wakumyankha iye.

40. Ndipo iye ananena ndi Aisrayeli onse, Inu mukhale mbali yina, ndipo me ndi Jonatani mwana wanga tidzakhala mbali yinanso. Ndipo anthuwo ananena ndi Sauli, Citani cimene cikukomerani.

41. Cifukwa cace Sauli ananena ndi Yehova, Mulungu wa Israyeli, muonetse coonadi. Ndipo maere anagwera Sauli ndi Jonatani; koma anthuwo anapulumuka.

42. Ndipo Sauli anati, Mucite maere pakati pa ine ndi Jonatani mwana wanga. Ndipo anagwera Jonatani.

43. Pamenepo Sauli ananena ndi Jonatani, Undiuze cimene unacita. Ndipo Jonatani anamuuza, nati, Zoonadi ndinangolawako uci pang'ono ndi nsonga ya ndodo inali m'dzanja langa: ndipo onani ndiyenera kufa.

44. Pamenepo Sauli anati, Mulungu andilange, naoniezereko, pakuti udzafa ndithu, Jonatani.

45. Ndipo anthuwo ananena ndi Sauli, Kodi Jonatani adzafa, amene anacititsa cipulumutso cacikuru ici m'Israyeli? Musatero. Pali Yehova, palibe tsitsi limodzi la pa mutu wace lidzagwa pansi, pakuti iye anagwirizana ndi Mulungu lero. Comweco anthuwo anapulumutsa Jonatani kuti angafe. Ndipo Sauli analeka kuwapitikitsa Afilistiwo;

46. ndi Afilistiwo anamuka ku malo a iwo okha.

47. Ndipo pamene Sauli atakhazikitsa ufumu wa pa Israyeli, iye anaponyana ndi adani ace onse pozungulira ponse, ndi Moabu, ndi ana a Amoni, ndi Edomu ndi mafumu a Zoba, ndi Afilisti; ndipo pali ponse anapotolokerapo, anawalanga.

48. Ndipo iye anakula mphamvu, nakantha Aamaleki, napulumutsa Aisrayeli m'manja a akuwawawanya.

49. Ndipo ana a Sauli ndiwo Jonatani, ndi Isivi, ndi Malikisuwa; ndi maina a ana akazi ace awm ndi awa: dzina la woyamba ndiye Merabu, ndi dzina la mng'ono wace ndiye Mikala;

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 14