Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 6:6-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anaitana ansembe, nanena nao, Senzani likasa la cipangano, ndi ansembe asanu ndi awiri anyamule mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga za nkhosa zamphongo, kutsogolera nazo likasa la Yehova.

7. Nati kwa anthu, Pitani, muzizungulira mudzi, ndi ankhondo ndi zida zao atsogolere likasa la Yehova.

8. Ndipo atanena kwa anthu Yoswa, ansembe asanu ndi awiri akunyamula mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga za nkhosa zamphongo pamaso pa Yehova, anapita naliza mphalasazo; ndipo likasa la cipangano ca Yehova linawatsata.

9. Ndipo okonzeka kunkhondo anatsogolera ansembe akuliza mphalasa, koma akudza m'mbuyo anatsata likasa, ansembe ali ciombere poyenda iwo.

10. Ndipo Yoswa analamulira anthu, ndi kuti, Musamapfuula, kapena kumveketsa mau anu, asaturuke konse mau m'kamwa mwanu, mpaka tsiku lakunena nanu ine, Pfuulani; pamenepo muzipfuula.

11. Ndipo anazungulitsa likasa la Yehova mudzi, kuzungulira kamodzi; pamenepo analowa kucigono, nagona m'mwemo.

12. Ndipo Yoswa analawira mamawa, ndi ansembe anasenza likasa la Yehova.

13. Ndipo ansembe asanu ndi awiri, akunyamula mphalasa zisanu ndi ziwiri zanyanga za nkhosa zamphongo ndi kutsogolera nazo likasa la Yehova, anayenda ciyendere naliza mphalasazo; ndi okonzeka kunkhondowo anawatsogolera, ndi akudza m'mbuyo anatsata likasa la Yehova, ansembe ali ciombere poyenda iwo.

14. Ndipo tsiku laciwiri anazungulira mudzi kamodzi, nabwera kucigono; anatero masiku asanu ndi limodzi.

15. Ndipo kunali, tsiku lacisanu ndi ciwiri analawira mamawa, mbandakuca, nazungulira mudzi mommuja kasanu ndi kawiri; koma tsiku lijalo anazungulira mudzi kasanu ndi kawiri.

16. Ndipo kunali, pa nthawi yacisanu ndi ciwiri, pamene ansembe analiza mphalasa, Yoswa anati kwa anthu, Pfuulani; pakuti Yehova wakupatsani mudziwo.

17. Koma mudziwo udzaperekedwa kwa Yehova ndi kuonongeka konse, uwu ndi zonse ziri m'mwemo; Rahabi yekha wadamayo adzakhala ndi moyo, iye ndi onse ali naye m'nyumba, cifukwa anabisa mithenga tinawatumawo.

18. Ndipo inu, musakhudze coperekedwaco, mungadziononge konse, potapa coperekedwaco; ndi kuononga konse cigono ca Israyeli ndi kucisautsa.

19. Koma siliva yense, ndi golidi yense, ndi zotengera za mkuwa ndi citsulo zikhala copatulikira Yehova; zilowe m'mosungira cuma ca Yehova.

20. Ndipo anthu anapfuula, naliza mphalasa ansembe; ndipo kunali, pamene anthu anamva kulira kwa mphalasa, anapfuula anthu ndi mpfuu yaikuru, niligwa linga pomwepo; nakwera anthu kulowa m'mudzi, yense kumaso kwace; nalanda mudziwo.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 6