Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 49:6-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Koma pambuyo pace ndidzabwezanso undende wa ana a Amoni, ati Yehova.

7. Za Edomu. Yehova wa makamu atero: Kodi m'Temani mulibenso nzeru? kodi uphungu wawathera akucenjera? kodi nzeru zao zatha psiti?

8. Thawani inu, bwerani, khalani mwakuya, inu okhala m'Dedani; pakuti ndidzatengera pa iye tsoka la Esau, nthawi yoti ndidzamlanga iye.

9. Akafika kwa inu akuchera mphesa, sadzasiya mphesa zokunkha? akafika usiku akuba, adzaononga mpaka kutha?

10. Pakuti ndambvula Esau, ndambvundukula, sadzatha kubisala; mbeu zace zaonongeka, ndi abale ace, ndi anansi ace, ndipo palibe iye.

11. Siya ana ako amasiye, Ine ndidzawasunga; akazi ako amasiye andikhulupirire Ine.

12. Pakuti Yehova atero: Taonani, iwo amene sanaweruzidwa kuti amwe cikho adzamwadi; kodi iwe ndiye amene adzakhala wosalangidwa konse? sudzakhala wosalangidwa, koma udzamwadi.

13. Pakuti ndalumbira, Pali Ine, ati Yehova, kuti Boma adzakhala cizizwitso, citonzo, copasuka, ndi citemberero; ndipo midzi yace yonse idzakhala yopasuka cipasukire.

14. Ndamva mthenga wa kwa Yehoya, ndipo mthenga watumidwa mwa amitundu, wakuti, Sonkhanani, mumdzere, nimuukire nkhondo.

15. Pakuti, caona, ndakuyesa iwe wamng'ono mwa amitundu, ndi wonyozedwa mwa anthu.

16. Koma za kuopsya kwako, kunyada kwa mtima wako kunakunyenga iwe, wokhala m'mapanga a thanthwe, woumirira msanje wa citunda, ngakhale usanja cisanja cako pamwamba penipeni ngati ciombankhanga, ndidzakutsitsa iwe kumeneko, ati Yehova.

17. Ndipo Edomu adzakhala cizizwitso; ndipo yense wakupitapo adzazizwa, ndipo adzatsonyera zobvuta zace zonse.

18. Monga m'kupasuka kwa Sodomu ndi Gomora ndi midzi inzace, ati Yehova, munthu ali yense sadzakhala m'menemo, mwana wa munthu ali yense sadzagona m'menemo.

19. Taona, wina adzakwerera mudzi wolimba ngati mkango wocokera ku Yordano wosefuka; koma dzidzidzi ndidzamthamangitsa amcokere; ndipo ali yense amene asankhidwa, ndidzamuika woyang'anira wace, pakuti wakunga Ine ndani? adzandiikira nthawi ndani? ndipo mbusa adzaima pamaso panga ndani?

20. Cifukwa cace tamvani uphungu wa Yehova, umene waupangira pa Edomu; ndi zimene walingalirira okhala m'Temani, ndithu adzawakoka, ana ang'ono a zoweta; ndithu adzayesa busa lao bwinja pamodzi nao.

21. Dziko lapansi linthunthumira ndi phokoso Ija kugwa kwao; pali mpfuu, phokoso lace limveka pa Nyanja Yofiira.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 49