Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezara 9:10-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo tsopano, Mulungu wathu, tidzanenanji pambuyo pa ici? pakuti tasiya malamulo anu,

11. amene munalamulira mwa atumiki anu aneneri ndi kuti, Dzikolo mumukako likhale colowa canu ndilo dziko lodetsedwa mwa cidetso ca anthu a m'maikomo, mwa zonyansa zao zimene zinalidzaza, kuyambira nsonga yina kufikira nsonga inzace ndi ucisi wao.

12. Cifukwa cace tsono, musamapereka ana anu akazi kwa ana ao amuna, kapena kutengera ana anu amuna ana ao akazi, kapena kufuna mtendere wao ndi kukoma kwao nthwawi yonse, kuti mukhale olimba, ndi kudya zokoma za m'dziko, ndi kulisiyira ana anu colowa ca ku nthawi yonse.

13. Ndipo zitatigwera zonsezi cifukwa ca nchito zathu zoipa ndi kuparamula kwathu kwakukuru; popeza inu Mulungu wathu mwatilanga moticepsera mphulupulu zathu, ndi ku tipatsa cipulumutso cotere;

14. kodi tidzabwereza kuphwanya malamulo anu, ndi kukwatana nayo mitundu ya anthu ocita zonyansa izi? Simudzakwiya nafe kodi mpaka mwatitha, ndi kuti pasakhale otsala kapena akupulumuka?

15. Yehova Mulungu wa Israyeli, Inu ndinu wolungama, popeza tinatsala opulumuka monga lero lino; taonani, tiri pamaso panu m'kuparamula kwathu; pakuti palibe wakuima pamaso panu cifukwa ca ici.

Werengani mutu wathunthu Ezara 9