Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 2:14-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo masiku amene tinayenda kucokera ku Kadesi Barinea, kufikira tidaoloka mtsinje wa Zeredi, ndiwo zaka makumi atatu mphambu zisanu ndi zitatu; kufikira utatha mbadwo wonse wa amuna ankhondo m'cigono, monga Yehova adawalumbirira.

15. Komanso dzanja la Yehova linatsutsana nao, kuwaononga m'cigono, kufikira adawatha.

16. Ndipo kunali, atatha kufa amuna onse ankhondo mwa anthu,

17. Yehova ananena ndi ine, ndi kuti,

18. Lero lomwe utumphe malire a Moabu, ndiwo Ari.

19. Ndipo pamene uyandikiza popenyana ndi ana a Amoni, usawabvuta, kapena kuutsana nao; popeza sindidzakupatsako dziko la ana a Amoni likhale lako lako; popeza ndinapatsa ana a Loti ili likhale lao lao.

20. (Ilinso aliyesa dziko la Arefai; Arefai anakhalamo kale; koma Aamoni awacha Azamzumi;

21. ndiwo anthu akuru, ndi ambiri, ndi atalitali, monga Aanaki; koma Yehova anawaononga pamaso pao; ndipo analanda dziko lao, nakhala m'malo mwao;

22. monga iye anacitira ana a Bsau, akukhala m'Seiri, pamene anaononga Ahori pamaso pao; ndipo analanda dziko lao, nakhala m'malo mwao kufikira lero lomwe.

23. Kunena za Aavi akukhala m'midzi kufikira ku Gaza, Akafitori, akufuma ku Kafitori, anawaononga, nakhala m'malo mwao.)

24. Uka, yenda ulendo wako, ndi kuoloka mtsinje wa Arinoni; taonani, ndapereka Sihoni mfumu ya Hesiboni, M-amori, ndi dziko lace m'dzanja lako; yamba kulilandira, ndi kuutsana naye nkhondo.

25. Tsiku lino ndiyamba kuopsetsa nawe ndi kucititsa mantha nawe anthu a pansi pa thambo lonse, amene adzamva mbiri yako, nadzanjenjemera, nadzawawidwa cifukwa ca iwe.

26. Ndipo ndinatuma amithenga ocokera ku cipululu ca Kedemoti kwa Sihoni mfumu ya Hesiboni ndi mau a mtendere, ndi kuti,

27. Ndipitire m'dziko mwako; ndidzatsata mseu, osapatuka ine ku dzanja lamanja kapena kulamanzere,

28. Undigulitse cakudya ndi ndarama, kuti ndidye; ndi kundipatsa madzi kwa ndarama, kuti ndimwe; cokhaci ndipitire coyenda pansi;

29. monga anandicitira ana a Esau akukhala m'Seiri, ndi Amoabu akukhala m'Ari; kufikira nditaoloka Yordano kulowa dziko limene Yehova Mulungu wathu atipatsa.

30. Koma Sihoni mfumu ya Hesiboni sanatilola kupitira kwao; popeza Yehova Mulungu wanu anaumitsa mzimu wace, nalimbitsa mtima wace, kuti ampereke m'dzanja lanu, monga lero lino.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 2