Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 16:10-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo mucitire Yehova Mulungu wanu madyerero a masabata, ndiwo msonkho waufulu wa dzanja lanu, umene mupereke monga Yehova Mulungu wanu akudalitsani.

11. Ndipo mukondwere pamaso pa Yehova Mulungu wanu, inu ndi ana anu amuna, ndi ana anu akazi, ndi anchito anu amuna, ndi anchito anu akazi, ndi Mlevi wokhala m'mudzi mwanu, ndi mlendo, ndi mwana wamasiye, ndi mkazi wamasiye, okhala pakati pa inu, m'malo amene Yehova Mulungu wanu adzasankha kukhalitsako dzina lace.

12. Ndipo mukumbukire kuti munali akapolo m'Aigupto; musamalire kucita malemba awa.

13. Mudzicitire madyerero a misasa masiku asanu ndi awiri, mutasunga za padwale ndi za mopondera mphesa;

14. nimukondwere m'madyerero mwanu, inu, ndi ana anu amuna, ndi ana anu akazi, ndi anchito anu amuna, ndi anchito anu akazi, ndi Mlevi, ndi mlendo, ndi mwana wamasiye, ndi mkazi wamasiye okhala m'mudzi mwanu.

15. Masiku asanu ndi awiri mucitire Yehova Mulungu wanu madyerero m'malo amene Yehova adzasankha; popeza Yehova Mulungu wanu adzakudalitsani m'zipatso zanu zonse, ndi m'nchito zonse za manja anu; nimukondwere monsemo.

16. Amuna onse azioneka pamaso pa Yehova Mulungu wanu m'malo amene iye adzasankha, katatu m'caka; pa madyerero a mkate wopanda cotupitsa, pa madyerero a masabata, ndi pa madyerero a misasa; ndipo asaoneke pamaso pa Yehova opanda kanthu;

17. apereke yense monga mwa mphatso ya m'dzanja lace, monga mwa mdalitso wa Yehova Mulungu wanu anakupatsani.

18. Mudziikire oweruza ndi akapitao m'inidzi yanu yonse imene Yehova Mulungu wanu akupatsani, monga mwa mapfuko anu; ndipo aweruze anthu ndi ciweruzo colungama.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 16