Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 8:5-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo polingirfrapo ine, taonani, wadza tonde wocokera kumadzulo, pa nkhope ya dziko lonse lapansi, wosakhudza nthaka; ndi mbuziyo inali ndi nyanga yooneka bwino pakati pa maso ace.

6. Ndipo anadzera nkhosa yamphongoyo yokhala ndi nyanga ziwiri, imene ndidaiona irikuima kumtsinje, naithamangira ndi mphamvu yace yaukali.

7. Ndipo ndinamuona wayandikira pafupi pa nkhosa yamphongo, nawawidwa mtima nayo, naigunda nkhosa yamphongo, natyola nyanga zace ziwiri; ndipo mphongoyo inalibe mphamvu yakuima pamaso pace, koma anaigwetsa pansi, naipondereza; ndipo panalibe wakupulumutsa mphongoyo m'dzanja lace.

8. Ndipo tondeyo anadzikulitsa kwakukuru, koma atakhala wamphamvu, nyanga yace yaikuru inatyoka; ndi m'malo mwace munaphuka nyanga zinai zooneka bwino, zoloza ku mphepo zinai za mlengalenga.

9. Ndipo mu imodzi ra izi munaphuka nyanga yaing'ono, imene inakula kwakukuru ndithu, kuloza kumwela, ndi kum'mawa, ndi ku dziko lokometsetsa.

10. Nikula, kufikira khamu la kuthambo; ndi zina za khamulo ndi za nyenyezi inazigwetsa pansi, nizipondereza.

11. Inde inadzikulitsa kufikira kwa kalonga wa khamulo, nimcotsera nsembe yopsereza yacikhalire; ndi pokhala malo ace opatulika panagwetsedwa.

12. Ndipo khamulo linaperekedwa kwa iyo, pamodzi ndi nsembe yopsereza yacikhalire mwa kulakwa kwace, nigwetsa pansi coonadi, nicita cifuniro cace, nikuzika.

13. Pamenepo ndinamva wina woyera, alikunena; ndi wina woyera anati kwa iye uja wanenayo, Masomphenya a nsembe yopsereza yacikhalire, ndi colakwa cakupululutsa ca kupereka malo opatulika ndi khamulo ziponderezedwe, adzakhala mpaka liti?

14. Nati kwa ine, Mpaka masiku zikwi ziwiri mphambu mazana atatu usana ndi usiku; pamenepo malo opatulika adzayesedwa olungama.

15. Ndipo kunali, nditaona masomphenyawo, ine Danieli ndinafuna kuwazindikira; ndipo taonani, panaima popenyana ndi ine ngati maonekedwe a munthu.

16. Ndipo ndinamva mau a munthu pakati pa magombe a Ulai, naitana, nati, Gabrieli, zindikiritsa munthuyu masomphenyawo.

17. Nayandikira iye poima inepo; atadza iye tsono ndinacita mantha, ndinagwa nkhope pansi; koma anati kwa ine, Zindikira, wobadwa ndi munthu iwe, pakuti masomphenyawo anena za nthawi ya cimariziro.

Werengani mutu wathunthu Danieli 8