Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 5:3-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Nabwera nazo zotengera zagolidi adazicotsa ku Kacisi wa nyumba ya Mulungu ya ku Yerusalemu, ndipo mfumu ndi akuru ace, akazi ace ndi akazi ace ang'ono, anamweramo.

4. Anamwa vinyo, nalemekeza milungu yagolidi, ndi yasiliva, yamkuwa, yacitsulo, yamtengo, ndi yamwala.

5. Nthawi yomweyo zinabuka zala za dzanja la munthu, nizinalemba pandunji pa coikapo nyali, pomata pa khoma la cinyumba ca mfumu; ndipo mfumu inaona nsonga yace ya dzanja lidalembalo.

6. Pamenepo padasandulika pa nkhope pace pa mfumu, ndi maganizo ace anamsautsa, ndi mfundo za m'cuuno mwace zinaguruka, ndi maondo ace anaombana.

7. Nipfuulitsa mfumu abwere nao openda, Akasidi, ndi alauli, Mfumu inalankhula, niti kwa anzeru a ku Babulo, Ali yense amene adzawerenga lemba ili, nadzandifotokozera kumasulira kwace, adzabvekedwa cibakuwa, ndi unyolo wagolidi m'khosi mwace, nadzakhala wolamulira wacitatu m'ufumuwu.

8. Pamenepo analowa anzeru onse a mfumu, koma sanakhoza kuwerenga lembalo, kapena kudziwitsa mfumu kumasulira kwace.

9. Ndipo mfumu Belisazara anabvutika kwambiri, ndi nkhope yace inasandulika, ndi akuru ace anathedwa nzeru.

10. Cifukwa ca mau a mfumu ndi akuru ace mkazi wamkuru wa mfumu analowa m'nyumba ya madyerero; mkazi wa mfumu ananena, nati, Mfumu, mukhale ndi moyo kosatha; asakubvuteni maganizo anu, ndi nkhope yanu isasandulike;

11. pali munthu m'ufumu mwanu mwa iye muli mzimu wa milungu yoyera; ndipo masiku a atate wanu munapezeka mwa iye kuunika, ndi luntha, ndi nzeru, ngati nzeru ya milungu; ndipo mfumu Nebukadinezara atate wanu, inde mfumu atate wanu anamuika akhale mkuru wa alembi, openda, Akasidi, ndi alauli;

Werengani mutu wathunthu Danieli 5