Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Samueli 14:6-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo mdzakazi wanu ndinali nao ana amuna awiri, ndipo awiriwa analimbana kumunda, panaboo wina wakuwaletsa, koma wina anakantha mnzace namupha.

7. Ndipo onani, cibale conse cinaukira mdzakazi wanu, ndi kuti, Upereke iye amene anakantha mbale wace, kuti timuphe cifukwa ca moyo wa mbale wace amene anamupha; koma pakutero adzaononga wolowa yemwe; comweco adzazima khara langa lotsala, ndipo sadzasiyira mwamuna wanga dzina kapena mbeu kunja kuno.

8. Ndipo mfumu inanena ndi mkaziyo, Pita ku nyumba yako, ndipo ndidzalamulira za iwe.

9. Ndipo mkazi wa ku Tekowayo ananena ndi mfumu, Mbuye wanga mfumu, mphulupulu ikhale pa ine ndi pa nyumba ya atate wanga; ndipo mfumu ndi mpando wacifumu wao zikhale zopanda cifukwa.

10. Ndipo mfumu inati, Ubwere naye kwa ine ali yense wakunena kanthu ndi iwe, ndipo iyeyo sadzakukhudzanso.

11. Nati iye, Mfumu mukumbukile Yehova Mulungu wanu kuti wolipsa mwazi asaonjeze kuononga, kuti angaononge mwana wanga. Niti iyo, Pali Yehova, palibe tsitsi limodzi la mwana wako lidzagwa pansi.

12. Pamenepo mkaziyo anati, Mulole mdzakazi wanu alankhule mau kwa mbuye wanga mfumu. Niti Iyo, Nena.

13. Ndipo mkaziyo anati, Cifukwa ninjinso munalingalira cinthu cotere pa anthu a Mulungu? pakuti pakulankhula mau awa mfumu ikunga woparamula, popeza mfumu siitumiza okamtenganso woingidwa wace.

14. Pakuti kufa tidzafa, ndipo tiri ngati madzi otayika pansi amene sakhoza kuwaolanso; ngakhale Mulungu sacotsa moyo, koma alingalira ngra yakuti wotayikayo asakhale womtayikira iye.

15. Cifukwa cace tsono cakuti ndadzanena mau awa ndi mbuye wanga mfumu, ndico kuti anthu anandiopsa ine; ndipo mdzakazi wanu ndinati, Ndilankhuletu ndi mfumu; kapena mfumu idzacita copempha mdzakazi wace.

16. Pakuti mfumu idzamvera ndi kupulumutsa mdzakazi wace m'dzanja la munthu wakufuna kundiononga ine pamodzi ndi mwana wanga, kuticotsa ku colowa ca Mulungu.

17. Ndipo mdzakazi wanu ndinati, Mau a mbuye wanga mfumu akhale opumulitsa; mbuye wanga mfumu ali ngati mthenga wa Mulungu, kuzindikira zabwino ndi zoipa; ndipo Yehova Mulungu wanu akhale nanu.

18. Pamenepo mfumu inayankha, ninena naye mkaziyo, Usandibisire kanthu ka zimene ndidzakufunsa iwe. Mkaziyo nati, Mbuye wanga mfumu anene.

19. Ndipo mfumuyo inati, Kodi Yoabu adziwana ndi iwe mwa izi zonse? Mkaziyo nayankha nati, Pali moyo wanu mbuye wanga mfumu, palibe kulewa ku dzanja lamanja, kapena kulamanzere kwa zonse mudazinena mbuye wanga mfumu; pakuti mnyamata wanu Yoabu ndiye anandiuza, naika mau onse awa m'kamwa mwa mdzakazi wanu.

20. Mnyamata wanu Yoabu anacita cinthu ici kuti asandulize mamvekedwe a mranduwo. Ndipo mbuye wanga ali wanzeru, monga ndi nzeru ya mthenga wa Mulungu, kudziwa zonse ziri m'dziko lapansi.

21. Ndipo mfumuyo inanena ndi Yoabu, Taonatu, ndacita cinthu ici; cifukwa cace, pita nubwere nayenso mnyamatayo Abisalomu.

22. Ndipo Yoabu anagwa nkhope yace pansi, namlambira, nadalitsa mfumuyo; nati Yoabu, Lero mnyamata wanu ndadziwa kuti munandikomera mtima, mbuye wanga mfumu, popeza mfumu yacita copempha mnyamata wace.

23. Comweco Yoabu ananyamuka namka ku Gesuri, nabwera naye Abisalomu ku Yerusalemu.

24. Ndipo mfumu inati, Apambukire ku nyumba yaiye yekha, koma asaone nkhope yanga. Comweco Abisalomu anapambukira ku nyumba ya iye yekha, wosaona nkhope ya mfumu.

25. Ndipo m'lsrayeli monse munalibe wina anthu anamtama kwambiri cifukwa ca kukongola kwace monga Abisalomu; kuyambira ku mapazi kufikira pakati pa mutu wace mwa iye munalibe cirema.

Werengani mutu wathunthu 2 Samueli 14