Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 6:21-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo mverani mapembedzero a kapolo wanu ndi a anthu anu Israyeli, popemphera iwo kuloza konkuno; ndipo mumvere Inu m'Mwamba mokhala Inumo, ndipo pakumva Inu, mukhululikire.

22. Munthu akacimwira mnansi wace, ndipo akamuikira lumbiro lakumlumbiritsa, ndipo akadzalumbira ku guwa lanu la nsembe, m'nyumba yino;

23. pamenepo mumvere m'Mwamba, nimucite ndi kuweruzira akapolo anu, kumtsutsa woipayo, ndi kumbwezera chimo lace, ndi kulungamitsa wolungamayo, kumbwezera monga mwa cilungamo cace.

24. Ndipo anthu anu Israyeli akawakantha mdani cifukwa ca kukucimwirani, nakabwerera iwowa ndi kubvomereza dzina lanu, ndi kupemphera, ndi kupembedzera pamaso panu m'nyumba yino;

25. pamenepo mumvere Inu m'Mwamba, nimukhululukire chimo la anthu anu Israyeli, ndi kuwabwezera ku dziko limene munapatsa makolo ao.

26. Mukatsekeka m'mwamba, mopanda mvula, cifukwa ca kukucimwirani; akapemphera iwo kuloza kumalo kuno, ndi kubvomereza dzina lanu, ndi kutembenuka kwa zoipa zao, pamene muwasautsa;

27. pamenepo mumvere Inu m'Mwamba, nimukhululukire chimo la akapolo anu, ndi la anthu anu Israyeli, mutawalangiza njira, yokoma ayenera kuyendamo, nimutumizire mvula dziko lanu limene munapatsa anthu anu likhale colowa cao.

28. Mukakhala njala m'dzikomo, mukakhala mliri, mukakhala cinsikwi, kapena cinoni, dzombe, kapena kapuce; akawamangira misasa adani ao, m'dziko la midzi yao; mukakhala mliri uli wonse, kapena nthenda iri yonse;

29. pemphero ndi pembedzero liri lonse likacitika ndi munthu ali yense, kapena ndi anthu anu onse Aisrayeli, akadziwa yense cinthenda cace, ndi cisoni cace, nakatambasulira manja ace kuloza ku nyumba iyi;

30. pamenepo mumvere m'Mwamba mokhala Inumo, nimukhululukire, ndi kubwezera ali yense monga mwa njira zace zonse, monga mudziwa mtima wace; pakuti Inu, Inu nokha, mudziwa mitima ya ana a anthu;

31. kuti aope Inu, kuyenda m'njira zanu masiku onse akukhala iwo m'dziko limene munapatsa makolo athu.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 6