Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 19:10-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Muzitero naye Hezekiya mfumu ya Yuda, kuti, Asakunyenge Mulungu wako amene umkhulupirira, ndi kuti, Yerusalemu sudzaperekedwa m'dzanja la mfumu ya Asuri.

11. Taona, udamva ico mafumu a Asuri anacitira maiko onse, ndi kuwaononga konse; ndipo uti upulumuke ndiwe kodi?

12. Kodi milunguyaamitundu inawalanditsa amene makolo anga anawaononga, ndiwo Gozani, ndi Hara Rezefi, ndi ana a Edeni okhala m'Telasara?

13. Iri kuti mfumu ya Hamati, ndi mfumu ya Aripadi, ndi mfumu ya mudzi wa Sefaravaimu, wa Hena, ndi Iva?

14. Ndipo Hezekiya analandira kalatayo ku dzanja la mithenga, namwerenga, nakwera Hezekiya kumka ku nyumba ya Yehova, namfunyulula pamaso pa Yehova.

15. Napemphera Hezekiya pamaso pa Yehova, nati, Yehova Mulungu wa Israyeli wakukhala pakati pa akerubi, Inu ndinu Mulungu mwini wace, Inu nokha, wa maufumu onse a dziko lapansi; munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.

16. Cherani khutu lanu, Yehova, nimumve; tsegulani maso anu, Yehova, nimupenye; ndipo imvani mau a Sanakeribu, amene anatumiza kutonza nao Mulungu wamoyo.

17. Zoona, Yehova, mafumu a Asuri anapasula amitundu ndi maiko ao,

18. naponya milungu yao kumoto; popeza sindiyo milungu koma yopanga anthu ndi manja ao, mtengo ndi mwala; cifukwa cace anaiononga.

19. Ndipo tsono, Yehova Mulungu wathu, mutipulumutse m'dzanja lace, kuti adziwe maufumu onse a dziko lapansi kuti Inu ndinu Yehova Mulungu, Inu nokha nokha.

20. Pamenepo Yesaya mwana wa Amozi anatumiza kwa Hezekiya, ndi, kuti, Atero Yehova Mulungu wa Israyeli, Condipempha iwe pa Sanakeribu mfumu ya Asuri ndacimva.

21. Mau a Yehova akumnenera iye ndi awa, Namwali mwana wamkazi wa Ziyoni akunyoza, akuseka mwana wamkazi wa Yerusalemu, akupukusira mutu pambuyo pako.

22. Ndiye yani wamtonza ndi kumcitira mwano? ndiye yani wamkwezera mau ndi kumgadamira maso ako m'mwamba? Ndiye Woyerayo wa Israyeli.

23. Watonza Yehova mwa mithenga yako, nuti, Ndi magareta anga aunyinji ndakwera pa misanje ya mapiri ku mbali zace za Lebano, ndipo ndidzagwetsa mikungudza yace yaitali, ndi mitengo yace yosankhika yar mlombwa, ndidzalowanso m'ngaka mwace mweni mweni, ku nkhalango zace za madimba.

24. Ndakapa, ndamwa madzi acilendo, ndi ku mapazi anga ndidzaphwetsa mitsinje yonse ya Aigupto,

25. Sunamva kodi kuti Ine ndinacicita kale lomwe, ndi kucipanga masiku akalekale? tsopano ndacifikitsa kuli iwe, uzikhala wakupasula imidzi yamalinga ikhale miunda ya mabwinja.

26. Cifukwa cace okhalamo ao anali ofok a manja, anaopsedwa, nacita manyazi, ananga udzu wa kuthengo, ndi msipu wauwisi, ndi udzu wa patsindwi, ndi tirigu wopserera asanakule.

27. Koma ndidziwa kukhala pansi kwako, ndi kuturuka kwako, ndi kulowa kwako, ndi kundizazira kwako.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 19