Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 17:6-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. nakuta msongolo wace ndi cobvala camkuwa, ndiponso pacikota pace panali nthungo yamkuwa.

7. Ndipo mtengo wa mkondo wace unali ngati mtanda woombera nsaru; ndi khali la mkondowo linalemera ngati masekeli mazana asanu ndi limodzi a citsulo; ndipo womnyamulira cikopa anamtsogolera.

8. Naima iye naitana makamu a nkhondo a Israyeli, nanena nao, Munaturukiranji kundandalitsa nkhondo yanu? Sindine Mfilisti kodi, ndi inu anyamata a Sauli? mudzisankhire munthu, atsikire kwa ine.

9. Akakhoza iyeyo kuponyana ndi ine ndi kundipha, tidzakhala ife akapolo anu; koma ine ndikamlaka, ndi kumupha, tsono mudzakhala inu akapolo athu, ndi kutitumikira ife.

10. Nati Mfilistiyo, Ine ndinyoza makamu a nkhondo a Israyeli lero; mundipatse munthu, kuti tilimbane ife awiri.

11. Ndipo pamene Sauli ndi Aisrayeli onse anamva mau ao a Mfilistiyo, anadodoma, naopa kwambiri.

12. Tsono Davide anali mwana wa M-efrati uja wa ku Betelehemu-Yuda, dzina lace ndiye Jese; ameneyu anali nao ana amuna asanu ndi atatu; ndipo m'masiku a Sauli munthuyo anali nkhalamba, mwa anthu.

13. Ndipo ana atatu akuru a Jese anatsata Sauli kunkhondoko; ndi maina ao a ana ace atatuwo adapita ku nkhondowo ndiwo Eliabu woyambayo, ndi mnzace womponda pamutu pace Abinadabu, ndi wacitatu Sama.

14. Ndipo Davide anali wotsiriza; ndi akuru atatuwo anamtsata Sauli.

15. Koma Davide akamuka kwa Sauli, nabwerera kudzadyetsa nkhosa za atate wace ku Betelehemu.

16. Ndipo Mfilistiyo anayandikira m'mawa ndi madzulo, nadzionetsera masiku makumi anai.

17. Ndipo Jese anati kwa Davide mwana wace, Uwatengere abale ako efa watirigu uyu wokazinga, ndi mikate iyi khumi, nuthamangire nazo kuzithando kwa abale ako;

18. nunyamule ncinci izi khumi zamase ukapatse mtsogoleri wa cikwi cao, nukaone m'mene akhalira abale ako, nulandire cikole cao,

19. Tsono Sauli, ndi iwowa, ndi anthu onse a Israyeli, anali m'cigwa ca Ela, ku nkhondo ya Afilisti.

20. Ndipo Davide anauka m'mamawa, nasiyira nkhosa wozisungira, nasenza zija, namuka, monga anamuuza Jese; ndipo iye anafika ku linga la magareta, napeza khamu lirikuturuka kunka poponyanira nkhondo lirikupfuula.

21. Ndipo Israyeli ndi Afilisti anandandalitsa nkhondo zao, khamu tina kuyang'anana ndi khamu lina.

22. Ndipo Davide anasiya akatundu ace m'dzanja la wosungira akatundu, nathamangira ku khamulo, nadza nalankhula abale ace.

23. Ndipo m'mene iye anali cilankhulire nao, onani cinakwerako ciwindaco, Mfilisti wa ku Gati, dzina lace ndiye Goliate, woturuka pakati pa mipambo ya Afilisti, nalankhula monga mau omwe aja; ndipo Davide anawamva.

24. Ndipo Aisrayeli onse, pakumuona munthuyo, anamthawa, naopa kwambiri.

25. Nati Aisrayeli, Kodi mwaona munthu uyu amene anakwera kuno? zoonadi iye anakwera kuti adzanyoze Israyeli, ndipo munthu wakumupha iye, mfumu idzamlemeza ndi cuma cambiri, nidzampatsa mwana wace wamkazi, nidzayesa nyumba ya atate wace yaufulu m'Israyeli.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 17