Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 11:30-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Ndipo Ahiyayo anagwira cobvala cace catsopano, nacing'amba khumi ndi pawiri.

31. Nati kwa Yerobiamu, Takwaya magawo khumi; popeza atero Yehova Mulungu wa Israyeli, Taona ndidzaung'amba ufumu m'dzanja la Solomo ndi kukupatsa iwe mafuko khumi.

32. Koma iye adzakhala nalo pfuko limodzi, cifukwa ca Davide mtumiki wanga, ndi ca Yerusalemu, mudzi umene ndinausankha m'mafuko onse a Israyeli.

33. Nditero popeza iwo anandisiya, napembedza Asitoreti mulungu wa Azidoni, ndi Kemosi mulungu wa Amoabu, ndi Milikomu mulungu wa ana a Amoni, osayenda m'njira zanga, kucita cimene ciyenera pamaso panga, ndi kusunga malemba anga ndi maweruzo anga, monga umo anatero Davide atate wace.

34. Koma sindidzalanda ufumu wonse m'dzanja lace, koma ndidzamkhalitsa mfumu masiku ace onse, cifukwa ca Davide mtumiki wanga amene uja ndinamsankha, cifukwa kuti anasunga malamulo anga ndi malemba anga.

35. Koma ndidzalanda ufumu m'dzanja la mwana wace, ndi kupatsa iwe mafuko khumi amene.

36. Ndipo ndidzamninkha mwana wace pfuko limodzi, kuti Davide mtumiki wanga akhale cikhalire ndi nyali pamaso panga m'Yerusalemu, mudzi umene ndinadzisankhira kuikapo dzina langa.

37. Ndipo ndidzakutenga iwe, ndipo udzacita ufumu monga umo ukhumbira moyo wako, nudzakhala mfumu ya Israyeli.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 11