11. Taonani anzace onse adzakhala ndi manyazi, ndi amisiri ace ndi anthu; asonkhane onse pamodzi, aimirire; adzaopa, iwo onse adzakhala ndi manyazi.
12. Wacipala acita zace ndi nsompho, nagwira nchito ndi makala, nafanizira fanolo ndi nyundo, nagwira nchito yace ndi mkono wace wamphamvu; inde, ali ndi njala, ndipo mphamvu zace zilephera; iye samwa madzi, nalefuka.
13. Mmisiri wa mitengo atambalitsa cingwe; nalilemba ndi colembera, nalikonza ndi ncerero, nalilemba ndi zolinganizira, nalifanizira monga maonekedwe a munthu, monga munthu wokongola, kuti likhale m'nyumba.
14. Iye adzidulira yekha mikungudza, natenga mtengo wambawa, ndi wathundu, ndi kudzisankhira yekha wina wa mitengo ya nkhalango; naoka mtengo wamlombwa, mvula niukulitsa.
15. Ndipo udzakhala kuti munthu autenthe; iye natengako, nauotha moto; inde auyatsa, naoca mkate; inde, apanga mlungu, naulambira, naupanga fano losema, naligwadira.
16. Iye atenthako mbali yina pamoto; ndi mbali yinayo adya nyama; akazinga zokazinga, nakhuta, inde, aotha moto, nati, Ha, ndakongonoka, ndauona moto.
17. Ndipo cotsalaco apanga mlungu, ngakhale fano lace losema; iye aligwadira, nalipembedza, nalipemphera nati, Ndipulumutse ine, cifukwa kuti ndinu mulungu wanga.
18. Iwo sadziwa, kapena kuzindikira, cifukwa pamaso pao papakidwa thope, kuti sangaone, ndi m'mitima mwao kuti sangadziwitse.