Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 8:7-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo woyamba anaomba, ndipo panakhala matalala ndi moto, zosanganiza ndi mwazi, ndipo anazitaya pa dziko lapansi; ndipo limodzi la magawo atatu a dziko lidapserera, ndipo limodzi la magawo atatu a mitengo lidapserera, ndipo msipu wonse udapserera.

8. Ndipo mngelo waciwiri anaomba, ndipo monga ngati phiri lalikuru lakupserera ndi mota Iinaponyedwa m'nyanja; ndipo limodzi la magawo atatu a nyanja linasanduka mwazi;

9. ndipo lidafa limodzi la magawo atatu a zolengedwa ziri m'nyanja, zokhala ndi moyo; ndipo limodzi la magawo atatu a zombo lidaonongeka.

10. Ndipo anaomba mngelo wacitatu, ndipo idagwa kucokera kumwamba nyenyezi yaikuru, yoyaka ngati muuni, ndipo idagwa pa limodzi la magawo atatu a mitsinje, ndi pa akasupe amadzi;

11. ndipo dzina lace la nyenyeziyo alicha Cowawa; ndipo limodzi la magawo atatu a madzi lidasanduka cowawa; ndipo anthu ambiri adafa pakumwa madzi, pakuti anasanduka owawa.

12. Ndipo mngelo wacinai anaomba, ndipo limodzi la magawo atatu a dzuwa linagwidwa, ndi limodzi la magawo atatu a mwezi, ndi limodzi la magawo atatu a nyenyezi; kuti limodzi la magawo ao atatu lidetsedwe, ndi kuti limodzi la magawo ace atatu a usana lisawale, ndi usiku momwemo.

13. Ndipo ndinaona, ndipo ndinamva ciombankhanga cirikuuluka pakati pa mwamba, ndi kunena ndi mau akuru, Tsoka, tsoka, tsoka, iwo akukhala padz'ko, cifukwa ca mau otsala a lipenga la angelo atatu asanaombe.

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 8