Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Cibvumbulutso 8:5-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo mngeloyo anatenga mbale ya zofukiza, naidzaza ndi mota wopara pa guwa la nsembe, nauponya pa dziko lapansi; ndipo panakhala mabingu, ndi mau, ndi mphezi, ndi cibvomezi.

6. Ndipo angelo asanu ndi awiri akukhala nao malipenga anadzikonzera kuti aombe.

7. Ndipo woyamba anaomba, ndipo panakhala matalala ndi moto, zosanganiza ndi mwazi, ndipo anazitaya pa dziko lapansi; ndipo limodzi la magawo atatu a dziko lidapserera, ndipo limodzi la magawo atatu a mitengo lidapserera, ndipo msipu wonse udapserera.

8. Ndipo mngelo waciwiri anaomba, ndipo monga ngati phiri lalikuru lakupserera ndi mota Iinaponyedwa m'nyanja; ndipo limodzi la magawo atatu a nyanja linasanduka mwazi;

9. ndipo lidafa limodzi la magawo atatu a zolengedwa ziri m'nyanja, zokhala ndi moyo; ndipo limodzi la magawo atatu a zombo lidaonongeka.

10. Ndipo anaomba mngelo wacitatu, ndipo idagwa kucokera kumwamba nyenyezi yaikuru, yoyaka ngati muuni, ndipo idagwa pa limodzi la magawo atatu a mitsinje, ndi pa akasupe amadzi;

Werengani mutu wathunthu Cibvumbulutso 8