Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

Malire a Efraimu

1. Ndipo gawo La ana a Yosefe linaturuka kucokera ku Yordano ku Yeriko, ku madzi a Yeriko kum'mawa, kucipululu, nakwera kucokera ku Yeriko kumka kumapiri ku Beteli;

2. naturuka ku Beteli kumka ku Luzi, napitirira kumka ku malire a Aariki, ku Atarotu;

3. natsikira kumadzulo kumka ku malire a Ayafeleti, ku malire a Beti-horoni wa kunsi, ndi ku Gezeri; ndi maturukiro ace anali kunyanja.

4. Motero ana a Yosefe, Manase ndi Efraimu analandira colowa cao,

5. Ndipo malire a ana a Efraimu, monga mwa mabanja ao, ndiwo: malire a colowa cao kum'mawa ndiwo Atarotu-Adara, mpaka Betihoroni wa kumtunda;

6. naturuka malire kumadzulo ku Mikametatu kumpoto; nazungulira malire kum'mawa kumka ku Taanatu-silo, naupitirira kum'mawa kwace kwa Yanoa:

7. natsika kucokera ku Yanoa, kumka ku Atarotu, ndi ku Naara, nafika ku Yeriko, naturuka ku Yordano.

8. Kuyambira ku Tapua malire anamuka kumadzulo ku mtsinje wa Kana; ndi maturukiro ace anali kunyanja. Ici ndi colowa ca pfuko la ana a Efraimu monga mwa mabanja ao;

9. pamodzi ndi midzi adaipatulira ana a Efraimu pakati pa colowa ca ana a Manase, midzi yonse pamodzi ndi miraga yao.

10. Ndipo a sanaingitsa Akanani akukhala m'Gezeri; koma Akanani anakhala pakati pa Efraimu, kufikira lero lino, nawasonkhera msonkho.