Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yoswa 13:16-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Malire ao anayambira ku Aroeri wokhala m'mphepete mwa cigwa ca Arinoni, ndi mudzi uli pakati pa cigwa ndi cidikha conse ca ku Medeba;

17. Hesiboni ndi midzi yace yonse yokhala pacidikha; Diboni, ndi Bamoto-baala ndi Betibaala-Meoni;

18. ndi Yahaza ndi Kedemotu, ndi Mefaata;

19. ndi Kinyataimu, ndi Sibima, ndi Zeretisahara, m'phiri la kucigwa;

20. ndi Beti-peori, ndi matsikiro a Pisiga, ndi Beti-yesimotu;

21. ndi midzi yonse ya kucidikha, ndi ufumu wonse wa Sihoni mfumu ya Aamori, wocita ufumu m'Hesiboni, amene Mose anamkantha pamodzi ndi akalonga a Midyani, Evi, ndi Rekemu, ndi Zuri, ndi Huri ndi Reba, akalonga a Sihoni, nzika za m'dziko.

22. Ana a Israyeli anaphanso ndi lupanga Balamu mwana wa Beori, mlauli uja, pamodzi ndi ena adawaphawo.

23. Ndipo malire a ana a Rubeni ndiwo Yordano ndi malire ace. Ndico colandira ca ana a Rubeni monga mwa mabanja ao, midzi yace ndi miraga yace.

24. Ndipo Mose anapatsira pfuko la Gadi, ana a Gadi, monga mwa mabanja ao.

25. Ndipo malire ao ndiwo Yazeri, ndi midzi yonse ya Gileadi, ndi dziko la ana a Amoni logawika pakati, mpaka ku Aroeri, wokhala cakuno ca Raba;

26. ndi kuyambira Hesiboni mpaka Ramati-Mizipe, ndi Betonimu; ndi kuyambira Mahanaimu mpaka malire a Dibiri;

27. ndipo m'cigwa Betiharamu, ndi Beti-nimra, ndi Sukoti, ndi Zafoni, cotsala ca ufumu wa Sihoni mfumu ya Hesiboni, Yoidano ndi malire ace, mpaka malekezero a nyanja ya Kinereti, tsidya lija la Yordano kum'mawa.

28. Ici ndi colowa ca ana a Gadi, monga mwa mabanja ao, midzi yace ndi miraga yace.

29. Mose anaperekanso colowa kwa pfuko la Manase logawika pakati, ndico ca pfuko la Manase logawika pakati monga mwa mabanja ao.

30. Ndipo malire ao anayambira ku Mahanaimu, Basana lonse, ufumu wonse wa Ogi mfumu ya ku Basana, ndi midzi yonse ya Yairi, yokhala m'Basana, midzi makumi asanu ndi limodzi;

31. ndi Gileadi logawika pakati, ndi Asitarotu ndi Edrei, midzi ya ufumu wa Ogi m'Basana, inali ya ana a Makiri mwana wa Manase, ndiwo ana a Makiri ogawika pakati, monga mwa mabanja ao.

32. Izi ndi zolowazi Mose anazigawira m'zidikha za Moabu, tsidya ilo la Yordano ku Yeriko, kum'mawa.

33. Koma pfuko la Levi, Mose analibe kulipatsa colowa: Yehova Mulungu wa lsrayeli, ndiye colowa cao, monga ananena nao.

Werengani mutu wathunthu Yoswa 13