Mitu

  1. 1
  2. 2
  3. 3
  4. 4
  5. 5
  6. 6
  7. 7
  8. 8
  9. 9
  10. 10
  11. 11
  12. 12
  13. 13
  14. 14
  15. 15
  16. 16
  17. 17
  18. 18
  19. 19
  20. 20
  21. 21
  22. 22
  23. 23
  24. 24
  25. 25
  26. 26
  27. 27
  28. 28
  29. 29
  30. 30
  31. 31
  32. 32
  33. 33
  34. 34
  35. 35
  36. 36
  37. 37
  38. 38
  39. 39
  40. 40
  41. 41
  42. 42

Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yobu 24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Wamphamvuyonse alekeranji kuikiratu nyengo?Ndi iwo omdziwa alekeranji kudziwa masiku ace?

2. Alipo akusendeza malire;Alanda gulu la zoweta, nazidyetsa.

3. Akankhizira kwao buru wa amasiye,Atenga ng'ombe ya mfedwa ikhale cikole.

4. Apambukitsa aumphawi m'njira;Osauka a padziko abisala pamodzi.

5. Taonani, ngati mbidzi za m'cipululuAturukira ku nchito zao, nalawirira nkufuna cakudya;Cipululu ciwaonetsera cakudya ca ana ao.

6. Atema dzinthu zao m'munda;Natola khunkha m'munda wampesa wa woipa.

7. Agona amarisece usiku wonse opanda cobvala,Alibe copfunda pacisanu.

8. Abvumbwa ndi mvula kumapiri,Nafukata thanthwe posowa pousapo.

9. Akwatula wamasiye kubere,Natenga cikole cobvala ca osauka;

10. Momwemo ayenda amarisece opanda cobvala,Nasenza mtolo wa dzinthu ali ndi njala.

11. M'kati mwa malinga a iwo aja ayenga mafuta;Aponda mphesa moponderamo, namva ludzu.

12. M'mudzi waukuru anthu abuula alinkufa;Ndi moyo wa iwo olasidwa upfuula;Koma Mulungu sasamalira coipaco.

13. Iwo ndiwo amene apikisana nako kuunika,Sadziwa njira zace,Sasunga mayendedwe ace.

14. Kukaca auka wambanda, napha wosauka ndi waumphawi;Ndi usiku asanduka mbala.

15. Ndipo diso la wacigololo liyombekezera cisisira,Ndi kuti, Palibe diso lidzandiona;Nabvala cophimba pankhope pace.

16. Kuli mdima aboola nyumba,Usana adzitsekera,Osadziwa kuunika.

17. Pakuti iwo onse auyesa m'mawa mthunzi wa imfa;Pakuti adziwa zoopsa za mthunzi wa imfa.

18. Atengedwa ngati coyandama pamadzi;Gawo lao litembereredwa padziko;Sadzalunjikanso njira ya minda yamphesa.

19. Cirala ndi dzuwa zitha madzi a cipale cofewa,Momwemo manda acita nao ocimwa.

20. M'mimba mudzamuiwala; mphutsi zidzamudya mokondwera.Sadzamkumbukilanso;Ndipo cosalungama cidzatyoledwa ngati mtengo.

21. Alusira cumba wosabala,Osamcitira wamasiye cokoma.

22. Mulungu awakhalitsa amphamvu mwa mphamvu yace;Iwo aukanso m'mene anayesa kuti sadzakhala ndi moyo.

23. Awalola akhale osatekeseka, ndipo alimbikapo;Koma maso ace ali pa njira zao.

24. Akwezeka; m'kamphindi kuti zi;Inde atsitsidwa, acotsedwa monga onse ena,Adutidwa ngati tirigu ngala zace.

25. Ndipo ngati si kutero, anditsutsa ndani kuti ndiri wabodza,Ndi kuyesa mau anga opanda pace?