Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 49:25-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Alekeranji kusiya mudzi wa cilemekezo, mudzi wa cikondwero canga?

26. Cifukwa cace anyamata ace adzagwa m'miseu yace, ndipo anthu onse a nkhondo adzatontholetsedwa tsiku lomwelo, ati Yehova wa makamu.

27. Ndipo Ine ndidzayatsa moto m'khoma la Damasiko, udzathetsa zinyumba za Beni-Hadadi.

28. Za Kedara, ndi za maufumu a Hazori, amene anawakantha Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo.Yehova atero: Ukani, kwerani ku Kedara, funkhani ana a kum'mawa.

29. Mahema ao ndi zoweta zao adzazilanda, adzadzitengera nsaru zocingira zao, ndi katundu wao yense, ndi ngamila zao; ndipo adzapfuulira iwo, Mantha ponse ponse.

30. Thawani inu, yendani kutari, khalani mwakuya, Inu okhala m'Hazori, ati Yehova; pakuti Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo anapangira uphungu pa inu, nakulingalirirani.

31. Nyamukani, kwererani mtundu wokhala ndi mtendere, wokhala osadera nkhawa, ati Yehova, amene alibe zitseko ndi mipiringidzo, okhala pa okha.

32. Ndipo ngamila zao zidzakhala zofunkha, ndi unyinji wa ng'ombe zao udzakhala wolanda; ndipo ndidzabalalitsira ku mphepo zonse iwo amene ameta m'mbali mwa tsitsi lao; ndipo ndidzatenga tsoka lao ku mbali zao zonse, ati Yehova.

33. Ndipo Hazori adzakhala mokhalamo ankhandwe, bwinja lacikhalire; simudzakhalamo munthu, simudzagonamo mwana wa munthu.

34. Mau a Yehova amene anafika kwa Yeremiya mneneri, onena za Elamu poyamba kulamulira Zedekiya mfumu ya Yuda, kuti,

35. Yehova wa makamu atero: Taonani, ndidzatyola uta wa Elamu, ndiwo mtima wa mphamvu yao.

36. Pa Elamu ndidzatengera mphepo zinai ku mbali zinai za mlengalenga, ndidzamwaza iwo ku mphepo zonsezo; ndipo sikudzakhala mtundu kumene opitikitsidwa a Elamu sadzafikako.

37. Ndipo ndidzacititsa Elamu mantha pamaso pa amaliwongo ao, ndi pamaso pa iwo ofuna moyo wao; ndipo ndidzatengera coipa pa iwo, mkwiyo wanga waukali, ati Yehova; ndipo ndidzatumiza lupanga liwalondole, mpaka nditawatha;

38. ndipo ndidzaika mpando wacifumu wanga m'Elamu, ndipo ndidzaononga pamenepo mfumu ndi akulu, ati Yehova.

39. Koma padzaoneka masiku akutsiriza, kuti ndidzabwezanso undende wa Elamu, ati Yehova.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 49