Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 23:23-40 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Kodi ndine Mulungu wa pafupi, ati Yehova, si Mulungu wa patari?

24. Kodi munthu angathe kubisala mobisika kuti ndisamuone iye? ati Yehova. Kodi Ine sindidzala kumwamba ndi dziko lapansi? ati Yehova.

25. Ndamva conena aneneri, amene anenera zonama m'dzina langa, kuti, Ndalota, ndalota.

26. Ici cidzakhala masiku angati m'mtima mwa aneneri amene anenera zonama; ndiwo aneneri a cinyengo ca mtima wao?

27. amene aganizira kuti adzaiwalitsa anthu anga dzina langa, ndi maloto ao amene anena munthu yense kwa mnansi wace, monga makolo ao anaiwala dzina limene ndimcha nalo Baala.

28. Mneneri wokhala ndi loto, anene loto lace; ndi iye amene ali ndi mau anga, anene mau anga mokhulupirika. Kodi phesi ndi ciani polinganiza ndi tirigu? ati Yehova.

29. Kodi mau anga safanafana ndi moto? ati Yehova, ndi kufanafana ndi nyundo imene iphwanya mwala?

30. Cifukwa cace, taonani, Ine ndidana ndi aneneri, ati Yehova, amene amaba mau anga, yense kumbera mnansi wace.

31. Taonani, Ine ndidana ndi aneneri, ati Yehova, amene acita ndi malilime ao, ndi kuti, Ati Iye.

32. Taonani, Ine ndidana ndi amene anenera maloto onama, ndi kuwafotokoza ndi kusokeretsa anthu anga ndi zonama zao, ndi matukutuku ao acabe; koma Ine sindinatuma iwo, sindinauza iwo; sadzapindulira konse anthu awa, ati Yehova.

33. Ndipo pamene anthu awa, kapena mneneri, kapena wansembe, adzakufunsa iwe, kuti, Katundu wa Yehova ndi ciani? pamenepo uziti kwa iwo, Katundu wanji? Ndidzakucotsani inu, ati Yehova.

34. Koma za mneneri, ndi wansembe, ndi anthu, amene adzati, Katundu wa Yehova, ndidzamlanga munthuyo ndi nyumba yace.

35. Mudzatero yense kwa mnansi wace, ndi yense kwa mbale wace, Yehova wayankha ciani? ndipo Yehova wanena ciani?

36. Ndipo katundu wa Yehova simudzachulanso konse; pakuti mau a munthu adzakhala katundu wace; pakuti mwasokoneza mau a Mulungu wamoyo, Yehova wa makamu, Mulungu wathu.

37. Uzitero kwa mneneri, Yehova wakuyankha ciani? ndipo Yehova wanenanji?

38. Koma ngati muti, Katundu wa Yehova, cifukwa cace Yehova atero: Cifukwa muti mau awa, Katundu wa Yehova, ndipo ndatuma kwa inu, kuti, Musati, Katundu wa Yehova;

39. cifukwa cace, taonani, ndidzakuiwalani inu konse, ndipo ndidzakucotsani, ndi mudzi umene ndinakupatsani inu ndi makolo anu, ndidzaucotsa pamaso panga;

40. ndipo ndidzakutengerani inu citonzo camuyaya, ndi manyazi amuyaya, amene sadzaiwalika.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 23