Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yeremiya 13:12-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Cifukwa cace uzinena ndi iwo mau awa: Atero Yehova, Mulungu wa Israyeli, Matumba onse adzadzazidwa ndi vinyo; ndipo adzati kwa iwe, Kodi sitidziwitsa bwino kuti matumba onse adzadzazidwa ndi vinyo?

13. Ndipo udzati kwa iwo, Atero Yehova, Taonani, ndidzadzaza ndi ciledzero onse okhala m'dziko muno, ngakhale mafumu onse amene akhala pa mpando wacifumu wa Davide, ndi ansembe, ndi aneneri, ndi onse okhala m'Yerusalemu.

14. Ndipo ndidzaphwanyanitsa wina ndi wina, atate ndi ana, ati Yehova; sindidzakhala ndi cisoni, sindidzapulumutsa, sindidzakhala ndi cifundo, cakuti ndisawaononge.

15. Tamvani inu, Cherani khutu; musanyade, pakuti Yehova wanena.

16. Lemekezani Yehova Mulungu wanu, kusanade, mapazi anu asanakhumudwe pa mapiri acizirezire; nimusanayembekeze kuunika, Ive asanasandutse kuunikaku mthunzi wa imfa, ndi kukuyesa mdima wa bii.

17. Koma ngati simudzamva, moyo wanga udzalira m'tseri cifukwa ca kunyada kwanu; diso langa lidzalira kwambiri, lidzagwa misozi, cifukwa zoweta za Yehova zagwidwa m'nsinga.

18. Nenani kwa mfumu ndi kwa amace wa mfumu, Dzicepetseni, khalani pansi; pakuti zapamtu zanu zagwa, korona wanu wokoma.

19. Midzi ya ku Mwera yatsekedwa, palibe wotsegulira. Yuda wonse wacotsedwa m'ndende wonsewo, wacotsedwa m'nsinga.

20. Tukulani maso anu, taonani iwo amene acokera kumpoto; ziri kuti zoweta zinapatsidwa kwa iwe, zoweta zako zokoma?

21. Udzanena ciani pamene adzaika abale ako akuru ako, pakuti iwe wekha wawalangiza iwo akukana iwe? kodi zowawa sizidzakugwira iwe monga mkazi wobala?

22. Ndipo ngati udzati m'mtima mwako, Zimenezi zandifikira ine cifukwa ninji? Cifukwa ca coipa cako cacikuru nsaru zako zoyesa mfula zasanduka mbudulira, ndi zithende zako zaphwetekwa.

23. Kodi angathe Mkusi kusanduliza khungu lace, kapena nyalugwe maanga ace? pamenepo mungathe inunso kucita zabwino, inu amene muzolowera kucita zoipa,

24. Cifukwa cace ndidzabalalitsa iwo, monga ziputu zakupita, ndi mphepo ya kucipululu.

Werengani mutu wathunthu Yeremiya 13