Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 16:17-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Ndipo musakhale munthu m'cihema cokomanako pakulowa iye kucita cotetezera m'malo opatulika, kufikira aturuka, atacita cotetezera yekha, ndi mbumba yace, ndi msonkhano wonse wa Israyeli.

18. Ndipo aturukire guwa la nsembe lokhala pamaso pa Yehova ndi kulicitira cotetezera; natengeko mwazi wa ng'ombeyo, ndi mwazi wa mbuziyo, ndi kuupaka pa nyanga za guwa la nsembe pozungulira.

19. Ndipo awazepo mwazi wina ndi cala cace kasanu ndi katatu; ndi kuliyeretsa ndi kulipatula kulicotsera zodetsa za ana a Israyeli.

20. Ndipo atatha kucitira cotetezera malo opatulika, ndi cihema cokomanako, ndi guwa la nsembe, abwere nayo mbuzi yamoyo;

21. ndipo Aroni aike manja ace onse awiri pamutu pa mbuzi yamoyo, ndi kubvomereza pa iyo mphulupulu zonse za ana a Israyeli, ndi zolakwa zao zonse, monga mwa zocimwa zao zonse; naike izi pamutu pa mbuziyo, ndi kuitumiza kucipululu ndi dzanja la munthu wompangiratu,

Werengani mutu wathunthu Levitiko 16