Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Levitiko 13:16-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Kapena mnofu wofiira ukasandukanso, nusandulika wotuwa, afike kwa wansembe,

17. ndi wansembe amuone, ndipo taonani, ngati nthenda yasandulika yotuwa, wansembe amuche woyera wanthendayo; ndiye woyera.

18. Ndipo pamene thupi liri ndi cironda pakhungu pace, ndipo capola,

19. ndipo padali cironda pali cotupa coyera, kapena cikanga cotuuluka, pamenepo acionetse kwa wansembe; ndipo wansembe aone,

20. ndipo taonani, ngati cioneka cakumba kubzola khungu, ndipo tsitsi lace lisanduka lotuwa, pamenepo wansembe amuche wodetsedwa; ndiyo nthenda yakhate yabuka m'cirondamo.

21. Koma wansembe akaciona, ndipo taonani, palibe tsitsi loyera pamenepo, ndipo sicinakumba kubzola khungu, koma cazimba, pamenepo wansembe ambindikiritse masiku asanu ndi awiri;

22. ndipo ngati capitirira khungu, wansembe amuche wodetsedwa; ndilo khate.

23. Koma ngati cikanga caima pomwepo, cosakula, ndico cipsera ca cironda; ndipo wansembe amuche woyera.

24. Kapena pamene thupi lidapsya ndi mota pakhungu pace, ndipo mnofu wofiira wakupsyawo usanduka cikanga cotuuluka, kapena cotuwa:

25. pamenepo wansembe acione; ndipo taonani, ngati tsitsi la cikanga lasanduka lotuwa, ndipo cioneka cakumba kubzola khungu; pamenepo ndilo khate lobuka m'kupsyamo; ndipo wansembe azimucha wodetsedwa ndi nthenda yakhate.

26. Koma akaonapo wansembe, ndipo taonani, mulibe tsitsi loyera m'cikangamo, ndipo sicikumba kubzola khungu, koma cazimba; pamenepo wansembe ambindikiritse masiku asanu ndi awiri;

27. ndipo wansembe amuone tsiku lacisanu ndi ciwiri; ngati cakula pakhungu, wansembe amuche wodetsedwa; ndiyo nthenda yakhate,

28. Ndipo ngati cikanga ciima pomwepo, cosakula pakhungu koma cazimba; ndico cotupa ca kupsya; ndipo wansembe amuche woyera; pakuti ndico cipsera ca kupsya.

29. Ndipo ngati mwamuna kapena mkazi ali ndi nthenda pamutu kapena pandebvu,

30. wansembe aziona nthenda; ndipo taonani, ngati ioneka yokumba kubzola khungu, ndipo pali tsitsi loyezuka lotetemera; pamenepo wansembe amuche wodetsedwa; ndiyo mfundu, ndilo khate la mutu kapena ndebvu.

Werengani mutu wathunthu Levitiko 13