Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 47:8-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo Farao anati kwa Yakobo, Masiku a zaka za moyo wanu ndi angati?

9. Ndipo Yakobo anati kwa Farao, Masiku a zaka za ulendo wanga ndi zaka zana limodzi kudza makumi atatu; masiku a zaka za moyo wanga ali owerengeka ndi oipa, sanafikire masiku a zaka za moyo wa makolo angam'masikua ulendowao.

10. Ndipo Yakobo anamdalitsa Farao, naturuka pamaso pa Farao.

11. Ndipo Yosefe anakhazika atate wace ndi abale ace, napatsa iwo pokhala m'dziko la Aigupto, m'dera lokometsetsa la m'dziko, m'dziko la Ramese, monga analamulira Farao.

12. Ndipo Yosefe anacereza atate wace ndi abale ace, ndi mbumba yonse ya atate wace ndi cakudya monga mwa mabanja ao.

13. Ndipo munalibe cakudya m'dziko lonse; pakuti njala inalimba kwambiri; cifukwa cace dziko la Aaigupto ndi dziko la Kanani unalefuka cifukwa ca njalayo.

14. Ndipo Yosefe anasonkhanitsa ndalama zonse anazipeza m'dziko la Aigupto ndi m'dziko la Kanani, za tirigu amene anagula; ndipo Yosefe anapereka ndalama ku nyumba ya Farao.

15. Ndipo zitatha ndalama zonse m'dziko la Aigupto ndi m'dziko la Kanani, Aaigupto onse anadza kwa Yosefe, nati, Mutipatse ife cakudya; tiferenji pamaso panu? zatsirizika ndalama.

16. Ndipo Yosefe anati, Mundipatse ng'ombe zanu: ndipo ndidzakupatsani inu mtengo wa ng'ombe zanu ngati ndalama zatsirizika.

17. Ndipo anadza nazo ng'ombe zao kwa Yosefe, ndipo Yosefe anapatsa iwo cakudya cosinthana ndi akavalo, ndi nkhosa, ndi ng'ombe, ndi aburu; ndipo anawadyetsa iwo ndi cakudya cosinthana ndi zoweta zao zonse caka cimeneco.

18. Citatha caka cimeneco, anadza kwa iye caka caciwiri, nati kwa iye, Sitibisira mbuyathu kuti ndalama zathu zonse zatha; ndipo zoweta za ng'ombe oza mbuyathu: palibe kanthu kotsala pamaso pa mbuyathu, koma matupi athu ndi maiko athu;

19. tiferenji pamaso panu, ife ndi dziko lathu? mutigule ife ndi dziko lathu ndi cakudya, ndipo ife ndi dziko lathu tidzakhala akapolo a Farao; ndipo mutipatse ife mbeu, kuti tikhale ndi moyo, tisafe, ndi kuti dziko lisakhale labwinja.

20. Ndipo Yosefe anamgulira Farao dziko lonse la Aigupto, cifukwa Aaigupto anagulitsa yense munda wace, cifukwa njala inakula pa iwo; ndipo dziko linakhala la Farao.

21. Tsono anthu, anasunthira iwo ku midzi kucokera kumphepete kwa malire a Aigupto kufikira kumphepete kwina kwace.

Werengani mutu wathunthu Genesis 47