Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Genesis 28:9-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. ndipo ananka kwa Ismayeli, naonjezera kwa akazi amene anali nao, natenga Mahalati mwana wamkazi wa Ismayeli mwana wa Abrahamu, mlongo wace wa Nebayoti akhalemkazi wace.

10. Ndipo Yakobo anacoka m'Beereseba, nanka ku Harana.

11. Ndipo anafika kumalo, nagona kumeneko usiku, cifukwa lidalowa dzuwa: ndipo anatenga mwala wa kumeneko, nauika pansi pa mutu wace, nagona tulo kumeneko.

12. Ndipo analota, taonani, makwerero anaima pansi, pamwamba pace ndipo padafikira kumwamba: ndipo, taonani, amithenga a Mulungu analinkukwera, analinkutsika pamenepo.

13. Taonani, Yehova anaima pamwamba pace, nati, Ine ndine Yehova, Mulungu wa Abrahamu atate wako, ndi Mulungu wa Isake; dziko limene ulinkugonamo ndidzakupatsa Iwe ndi mbeu zako;

14. mbeu zako zidzakhala monga pfumbi lapansi, ndipo udzabalalikira kumadzulo ndi kum'mawa ndi kumpoto ndi kumwera: mwa iwe ndi mu mbeu zako mabanja onse a dziko lapansi adzadalitsidwa.

15. Taonani, Ine ndiri pamodzi ndi iwe, ndipo ndidzakusunga iwe konse kumene upitako, ndipo ndidzakubwezanso iwe ku dziko lino; cifukwa kuti sindidzakusiya iwe, kufikira kuti nditacita cimene ndanena nawe.

16. Ndipo Yakobo anauka m'tulo tace, nati, Ndithu, Yehova ali mommuno; ndipo sindinadziwe.

17. Ndipo anaopa, nati, Poopsya pompano! pompano ndipo pa nyumba ya Mulunga, si penai, pompano ndipo pa cipata ca kumwamba.

18. Yakobo ndipo anauka m'mamawa, natenga mwala umene anaika pansi pa mutu wace, nauimiritsa, nathira mafuta pamtu pace.

19. Ndipo anacha dzina la pamenepo Beteli; pakuyamba dzina lace la mudziwo ndi Luzi.

Werengani mutu wathunthu Genesis 28