Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Ezara 7:15-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. ndi kumuka nazo siliva ndi golidi, zimene mfumu ndi aphungu ace, anapereka mwaufulu kwa Mulungu wa Israyeli, mokhala mwace muli m'Yerusalemu,

16. pamodzi ndi siliva ndi golidi ziri zonse ukazipeza m'dziko lonse la ku Babulo, pamodzi ndi copereka caufulu ca anthu, ndi ca ansembe, akuperekera mwaufulu nyumba ya Mulungu wao iri ku Yerusalemu;

17. m'mwemo uzifulumira kugula ndi ndalama iyi ng'ombe, nkhosa zamphongo, ana a nkhosa, pamodzi ndi nsembe zao zaufa, ndi nsembe zao zothira; ndi kuzipereka pa guwa la nsembe la nyumba ya Mulungu wanu yokhala ku Yerusalemu.

18. Ndipo ciri conse cidzakomera iwe ndi abale ako kucita nazo siliva ndi golidi zotsala, ici mucite monga mwa cifuniro ca Mulungu wanu.

19. Ndipo zipangizozo akupatsa za utumiki wa nyumba ya Mulungu wako, uzipereka pamaso pa Mulungu wa ku Yerusalemu.

20. Ndi zina zotsala zakusowa nyumba ya Mulungu wako, zikayenera uzipereke, uzipereke zocokera ku nyumba ya cuma ca mfumu.

21. Ndipo ine Aritasasta, mfumu ine, ndilamulira osunga cuma onse okhala tsidya lija la mtsinjewo, kuti ciri conse akupemphani Ezara wansembe, mlembi wa lamulo la Mulungu wa Kumwamba, cicitike mofulumira;

22. mpaka matalente a siliva zana limodzi, ndi miyeso ya tirigu zana limodzi, ndi miyeso ya vinyo zana limodzi, ndi miyeso ya mafuta zana limodzi, ndi mcere wosauwerenga.

23. Ciri conse Mulungu wa Kumwamba acilamulire cicitikire mwacangu nyumba ya Mulungu wa Kumwamba; pakuti padzakhaliranji mkwiyo pa ufumu wa mfumu ndi ana ace?

24. Tikudziwitsaninso kuti sikudzaloledwa kusonkhetsa ali yense wa ansembe, ndi Alevi, oyimbira, odikira, Anetini, kapena anchito a nyumba iyi ya Mulungu msonkho, thangata, kapena msonkho wa panjira.

25. Ndipo iwe Ezara monga mwa nzeru za Mulungu wako iri m'dzanja lako, uike nduna, ndi oweruza mirandu, aweruze anthu onse ali tsidya lija la mtsinje, onse akudziwa malamulo a Mulungu wako; ndi wosawadziwayo umphunzitse.

26. Ndipo ali yense wosacita lamulo la Mulungu wako, ndi lamulo la mfumu, mlandu umtsutse msanga, ngakhale kumupha, kapena kumpitikitsa m'dziko, kapena kumlanda cuma cace, kapena kummanga m'kaidi.

Werengani mutu wathunthu Ezara 7