Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 7:16-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo mudzatha mitundu yonse ya anthu amene Yehova Mulungu wanu adzapereka kwa inu; diso lanu lisawacitire cifundo; musamatumikira milungu yao; pakuti uku kudzakucitirani msampha.

17. Mukadzanena m'mtima mwanu, Amitundu awa andicurukira; ndikhoza bwanji kuwapitikitsa?

18. musamawaopa; mukumbukile bwino cimene Yehova Mulungu wanu anacitira Farao, ndi Aigupto wonse;

19. mayesero akuru maso anu anawapenya, ndi zizindikilo ndi zozizwa, ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka, zimene Yehova Mulungu wanu anakuturutsani nazo; Yehova Mulungu wanu adzatero nayo mitundu yonse ya anthu imene muwaopa.

20. Komanso Yehova Mulungu wanu adzatumiza mabvu pakati pao, kufikira ataonongeka otsalawo, ndi akubisala pamaso panu.

21. Musamaopa pamaso pao; popeza Yehova Mulungu wanu ali pakati pa inu, Mulungu wamkuru ndi woopsa.

22. Ndipo Yehova Mulungu wanu adzataya amitundu awa pang'ono pang'ono; simuyenera kuwaononga msanga, kuti zingakucurukireni zirombo.

23. Koma Yehova Mulungu wanu adzawapereka pamaso panu, nadzawapitikitsa ndi kupitikitsa kwakukuru, kufikira ataonongeka.

24. Adzaperekanso mafumu ao m'dzanja mwanu, ndipo muwafafanize maina ao pansi pa thambo; palibe munthu mmodzi adzaima pamaso panu, kufikira mutawaononga,

25. Mafano osema a milungu yao muwateothe ndi moto; musamasirira siliva ndi golidi ziri pa iwo, kapena kudzitengera izi; mungakodwe nazo; pakuti izi zinyansira Yehova Mulungu wanu.

26. Musamalowa naco conyansaci m'nyumba mwanu, kuti mungaonongeke konse pamodzi naco; muziipidwa naco konse, ndi kunyansidwa naco konse; popeza ndi cinthu coyenera kuonongeka konse.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 7