Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Deuteronomo 11:5-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. ndi cimene anakucitirani m'cipululu, kufikira munadza kumalo kuno;

6. ndi cimene anacitira Datani ndi Abiramu, ana a Eliabu, mwana wa Rubeni; muja nthaka inatsegula pakamwa pace, ndi kuwameza iwo, ndi mabanja ao, ndi mahema ao, ndi za moyo zonse zakuwatsata pakati pa Israyeli wonse.

7. Koma maso anu anapenya nchito yonse yaikuru ya Yehova anaicita.

8. Potero muzisunga malamulo onsewa ndikuuzani lero lino, kuti mukhale amphamvu, ndi kulowa ndi kulandira dziko, limene mumkako kulilandira;

9. ndi kuti masiku anu acuruke m'dziko limene Yehova analumbirira makolo anu, kuti adzawapatsa iwo ndi mbeu zao, dziko moyenda mkaka ndi uci ngati madzi.

10. Pakuti dziko limene mumkako kulilandira ndi losanga dziko la Aigupto lija mudaturukako, kumene kuja munafesa mbeu zanu, ndi kuzithirira ndi phazi lanu, monga munda watherere;

11. koma dziko limene mumkako kulilandira ndilo dziko la mapiri ndi zigwa; limamwa madzi a mvula ya kumwamba;

12. ndilo dziko loti Yehova Mulungu wanu alisamalira, maso a Yehova Mulungu wanu akhalapo cikhalire, kuyambira caka mpaka kutsiriza caka.

13. Ndipo kudzakhala mukasamalira cisamalire malamulo anga amene ndikuuzani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu, ndi kumtumikira ndi mtima wanu wonse, ndi moyo wanu wonse,

14. ndidzapatsa mvula ya dziko lanu m'nyengo yace, ya myundo ndi ya masika, kuti mutute tirigu wanu, ndi vinyo wanu, ndi mafuta anu.

15. Ndipo ndidzapatsa msipu wa zoweta zanu podyetsa panu; mudzadyanso nimudzakhuta.

16. Dzicenjerani nokha, angacete mitima yanu, nimungapatuke, ndi kutumikira milungu yina, ndi kuipembedza;

17. ndi kuti Mulungu angapse mtima pa inu, a nangatseke kumwamba, kuti isowe mvula, ndi kuti nthaka isapereke zipatso zace; ndi kuti mungaonongeke msanga m'dziko lokomali Yehova akupatsani.

18. Cifukwa cace muzisunga mau anga awa mumtima mwanu ndi m'moyo mwanu; ndi kuwamanga ngati cizindikilo pamanja panu; ndipo zikhale zapamphumi pakati pa maso anu.

19. Ndipo muziwaphunzitsa ana anu, ndi kuwalankhula awa pokhala inu pansi m'nyumba mwanu, ndi poyenda inu panjira, ndi pogona inu pansi, ndi pakuuka inu pomwe.

20. Ndipo muziwalembera pa mphuthu za nyumba zanu, ndi pa zipata zanu;

21. kuti masiku anu ndi masiku a ana anu acuruke m'dziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzawapatsali, monga masiku a thambo liri pamwamba pa dziko.

22. Pakuti mukasunga cisungire malamulo awa onse amene ndikuuzani kuwacita; kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda m'njira zace zonse, ndi kummamatira;

23. Yehova adzapitikitsa amitundu awa onse pamaso panu, ndipo mudzalanda amitundu akuru ndi amphamvu oposa inu.

Werengani mutu wathunthu Deuteronomo 11