Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Danieli 9:4-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo ndinapemphera kwa Yehova Mulungu wanga ndi kubvomereza, ndi kuti, Ambuye Mulungu wamkuru ndi woopsa, wakuwasungira pangano ndi cifundo iwo akukukondani, ndi kusunga malamulo anu,

5. tacimwa, tacita mphulupulu, tacita zoipa, tapanduka, kupambuka ndi kusiya maneno anu ndi maweruzo anu;

6. sitinamvera atumiki anu aneneri, amene ananena m'dzina lanu kwa mafumu athu, akalonga athu, makolo athu, ndi anthu onse a m'dziko.

7. Ambuye, cilungamo nca Inu, koma kwa ife manyazi a nkhope yathu, monga lero lino; kwa anthu a Yuda, ndi kwa okhala m'Yerusalemu, ndi kwa Aisrayeli onse okhala pafupi ndi okhala kutali, ku maiko onse kumene mudawaingira, cifukwa ca kulakwa kwao anakulakwirani nako.

8. Ambuye, kwa ife kuli manyazi a nkhope yathu, kwa mafumu athu, kwa akalonga athu, ndi kwa makolo athu; pakuti takucimwirani.

9. Ambuye Mulungu wathu ndiye wacifundo, ndi wokhululukira; pakuti tampandukira Iye;

10. sitinamvera mau a Yehova Mulungu wathu, kuyenda m'malamulo ace anatiikirawo pamaso pathu, mwa atumiki ace aneneri.

11. Inde Israyeli yense walakwira cilamulo canu, ndi kupambuka, kuti asamvere mau anu; cifukwa cace temberero lathiridwa pa ife, ndi Ilumbiro lolembedwa m'cilamulo ca Mose mtumiki wa Mulungu; pakuti tamcimwira.

12. Ndipo anakwaniritsa mau ace adanenawo, kutitsutsa ife ndi oweruza athu otiweruza, ndi kutitengera coipa cacikuru; pakuti pansi pa thambo lonse sipanacitika monga umo panacitikira Yerusalemu.

13. Monga mulembedwa m'cilamulo ca Mose coipa ici conse catidzera; koma sitinapepeza Yehova Mulungu wathu, ndi kubwera kuleka mphulupulu zathu, ndi kucita mwanzeru m'coonadi canu.

14. Cifukwa cace Yehova wakhala maso pa coipaco, ndi kutifikitsira ico; pakuti Yehova Mulungu wathu ali wolungama mu nchito zace zonse azicita; ndipo sitinamvera mau ace.

15. Ndipo tsopano, Ambuye Mulungu wathu, amene munaturutsa anthu anu m'dziko la Aigupto ndi dzanja lamphamvu, ndi kudzitengera mbiri monga lero lino, tacimwa, tacita coipa.

16. Ambuye, monga mwa cilungamo canu conse, mkwiyo wanu ndi ukali wanu zitembenuketu, zicoke ku mudzi wanu Yerusalemu, phiri lanu lopatulika; pakuti mwa zocimwa zathu, ndi mphulupulu za makolo athu, Yerusalemu ndi anthu anu asanduka cotonza ca onse otizungulira.

17. Ndipo tsopano, Mulungu wathu, mumvere pemphero la mtumiki wanu, ndi mapembedzero ace, nimuwalitse nkhope yanu pa malo anu opatulika amene ali opasuka, cifukwa ca Ambuye,

18. Mulungu wanga, cherani khutu, nimumvere, tsegulani maso anu, nimupenye zopasuka zathu, ndi mudzi udachedwawo dzina lanu; pakuti sititula mapembedzero athu pamaso panu, cifukwa ca nchito zathu zolungama, koma cifukwa ca zifundo zanu zocuruka.

19. Ambu ye, imvani; Ambuye, khululukirani; Ambuye, mverani nimucite; musacedwa, cifukwa ca inu nokha, Mulungu wanga; pakuti mudzi wanu ndi anthu anu anachedwa dzina lanu.

20. Ndipo pakunena ine, ndi kupemphera, ndi kubvomereza cimo langa, ndi cimo la anthu amtundu wanga Israyeli, ndi kutula cipembedzero canga pamaso pa Yehova Mulungu wanga, cifukwa ca phiri lopatulika la Mulungu wanga;

21. inde pakunena ine m'kupemphera, munthu uja Gabrieli, amene ndidamuona m'masomphenya poyamba paja, anauluka mwaliwiro nandikhudza ngati nthawi yakupereka nsembe ya madzulo.

Werengani mutu wathunthu Danieli 9