Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 18:10-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo Zedekiya mwana wa Kenana anadzisulira nyanga zacitsulo, nati, Atero Yehova, Ndi izi udzagunda Aaramu mpaka adatha psiti.

11. Ndi aneneri onse ananenera momwemo, ndi kuti, Kwerani ku Ramoti Gileadi, mudzapindulako; pakuti Yehova adzaupereka m'dzanja la mfumu.

12. Ndipo mthenga wakukaitana Mikaya ananena naye, ndi kuti, Taonani, mau a aneneri anenera mfumu cokoma ngati m'kamwa m'modzi; mau anu tsono akhaletu ngati amodzi a iwowa, nimunene cokoma.

13. Nati Mikaya, Pali Yehova, conena Mulungu wanga ndidzanena comweci.

14. Pamene anafika kwa mfumu, mfumu inanena naye, Mikaya timuke ku Ramoti Gileadi kunkhondo kodi, kapena ndileke? Nati iye, Kwerani, mudzacita mwai; ndipo adzaperekedwa m'dzanja lanu.

15. Ndipo mfumu inati naye, Ndikulumbiritse kangati kuti unene nane coonadi cokha cokha m'dzina la Yehova?

16. Nati iye, Ndinaona Aisrayeli onse obalalika pamapiri ngati nkhosa zopanda mbusa; nati Yehova, Awa alibe mbuye wao, abwerere yense ku nyumba yace mumtendere.

17. Ndipo mfumu ya Israyeli inati kwa Yehosafati, Sindinakuuzani kuti sadzandinenera zabwino koma zoipa?

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 18