Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 6:7-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Cifukwa cace tsono, tengani, nimukonze gareta latsopano, ndi ng'ombe ziwiri zamkaka, zosalawa goli cikhalire, ndipo mumange ng'ombezo pagareta, muzicotsere ana ao kunka nao kwanu;

8. ndipo mutenge likasa la Yehova, nimuliike pagaretapo; nimuike zokometsera zagolidi, zimene muzipereka kwa iye ngati nsembe yoparamula, m'bokosi pam bali pace; nimulitumize licoke.

9. Ndipo muyang'anire, ngati likwera pa njira ya malire ace ace ku Betisemesi, iye anaticitira coipa ici cacikuru; koma likapanda kutero, tidzadziwapo kuti dzanja limene linatikantha, siliri lace; langotigwera tsokali.

10. Ndipo anthuwo anatero; natenga ng'ombe ziwiri zamkaka, nazimanga pagareta, natsekera anao kwao;

11. naika likasa la Yehova pagaretapo, ndi bokosi m'mene munali mbewa zagolidi ndi zifanizo za mafundo ao.

12. Ndipo ng'ombezo zinatsata njira yolunjika ku Betisemesi, niziyenda mumseu, zirikulira poyenda; sizinapambukira ku dzanja lamanja, kapena kulamanzere; ndipo mafumu a Afilisti anazitsatira kufikira ku malire a Betisemesi.

13. Ndipo a ku Betisemesi analikumweta tirigu wao m'cigwamo; natukula maso ao, naona likasalo, nakondwerapakuliona.

14. Ndipo garetalo linafika m'munda wa Yoswa wa ku Betisemesi, ndi kuima momwemo, pa mwala waukuru; ndipo anawaza matabwa a garetalo, nazipereka ng'ombezo nsembe yopsereza kwa Yehova.

15. Ndipo Alevi anatsitsa likasa la Yehova, ndi bokosi linali nalo, m'mene munali zokometsera zagolidi, naziika pa mwala waukuruwo; ndipo anthu a ku Betisemesi anapereka nsembe zopsereza, naphera nsembe kwa Yehova tsiku lomwelo.

16. Ndipo pamene mafumu asanu a Afilisti anaonerako, anabwerera kunka ku Ekroni tsiku lomwelo.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 6