Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 19:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo pamene anauza Sauli, iye anatumiza mithenga yina; koma iyonso inanenera. Ndipo Sauli anatumiza mithenga kacitatu, nayonso inanenera.

22. Pamenepo iyenso anamuka ku Rama, nafika ku citsime cacikuru ciri ku Seku, nafunsa Dati, Samueli ndi Davide ali kuti? Ndipo wina anati, Taonani, ali ku Nayoti m'Rama.

23. Ndipo anapita komweko ku Nayoti m'Rama; ndi mzimu wa Mulungu unamgwera iyenso; ndipo anapitirira, nanenera, mpaka anafika ku Nayoti m'Rama.

24. Ndiponso anabvula zobvala zace, naneneranso pamaso pa Samueli nagona wamarisece usana womwe wonse, ndi usiku womwe wonse. Cifukwa cace amati, Kodi Saulinso ali pakati pa aneneri?

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 19