Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 17:27-37 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ndipo anthuwo anamyankha motero, nati, Adzamcitira munthu wakumupha iye mwakuti mwakuti.

28. Ndipo Eliabu mkuru wace anamumva iye alikulankhula ndi anthu; ndipo Eliabu anapsa mtima ndi Davide, nati, Unatsikiranji kuno? ndi nkhosa zija zowerengeka unazisiya ndi yani, m'cipululu muja? Ine ndidziwa kudzikuza kwako ndi kuipa kwa mtima wako; pakuti watsika kuti udzaone nkhondoyi.

29. Ndipo Davide anati, Ndacitanji tsopano? Palibe cifukwa kodi?

30. Napotolokera iye kwa munthu wina, nalankhula mau omwewo; ndipo anthu anamyankhanso monga momwemo.

31. Ndipo pamene mau adanena Davide anamveka, anawapitiriza kwa Sauli; ndipo iye anamuitana.

32. Ndipo Davide anati kwa Sauli, Asade nkhawa munthu ali yense cifukwa ca iyeyo; ine kapolo wanu ndidzapita kuponyana ndi Mfilisti uyu.

33. Ndipo Sauli anati kwa Davide, Sukhoza iwe kukomana ndi Mfilisti uyu kukaponyana naye; pakuti iwe ndiwe mnyamata, koma iye anazolowera nkhondo kuyambira ubwana wace.

34. Ndipo Davide anati kwa Sauli, Ine kapolo wanu ndinalikusunga nkhosa za atate wanga; ndipo pakubwera mkango, mwina cimbalangondo ndi kutenga nkhosa ya gululo,

35. ndinacithamangira, ndi kucikantha, ndi kuiturutsa m'kamwa mwace; ndipo pamene cinaneliukira, ndinagwira cowa lace ndi kucikantha ndi kucipha.

36. Ine kapolo wanu ndinapha mkango ndi cimbalangondo zonse ziwiri; ndipo Mfilisti uyu wosadulidwa adzakhala ngati mmodzi wa izo, popeza wanyoza makamu a Mulungu wamoyo.

37. Nati Davide, Yehova wakundipulumutsa pa mphamvu ya mkango, ndi mphamvu ya cimbalangondo, Iyeyu adzandipulumutsa m'dzanja la Mfilisti uyu, Ndipo Sauli anati kwa Davide, Muka, Yehova akhale nawe.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 17