Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 10:6-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. ndipo Mzimu wa Yehova udzagwera inu kolimba, nanunso mudzanenera pamodzi nao, nimudzasandulika munthu wina.

7. Ndipo zitakufikirani zizindikilo izi mudzacita monga mudzaona pocita, pakuti Mulungu ali nanu.

8. Ndipo mudzatsika patsogolo pa ine kunka ku Giligala; ndipo, taonani, ndidzatsikira kwa inu kukapereka zopsereza, ndi kuphera nsembe zamtendere. Mutsotsepo masiku asanu ndi awiri kufikira ndikatsikira kwa inu ndi kukudziwitsani cimene mudzacita.

9. Ndipo kunali, pamene iye anapotoloka kuti alekane ndi Samueli, Mulungu anampatsa mtima wina watsopano; ndipo zizindikilo zija zonse zinacitika tsiku lija.

10. Ndipo pamene anafika kucitunda kuja, onani, gulu la aneneri linakomana naye; ndi Mzimu wa Mulungu unamgwera mwamphamvu, iye nanenera pakati pao,

11. Ndipo kunali, kuti onse amene anamdziwiratu kale, pakuona ici cakuti, onani, iye ananenera pamodzi ndi aneneri, anati wina ndi mnzace, Ici nciani cinamgwera mwana wa Kisi? Kodi Saulinso ali mwa aneneri?

12. Ndipo munthu wina wa komweko anayankha nati, Ndipo atate wao ndiye yani? Cifukwa cace mauwa anakhala ngati mwambi, Kodi Saulinso ali mwa aneneri?

13. Ndipo pamene adatha kunenera anafika kumsanjeko.

14. Ndipo mbale wa atate wace wa Sauli ananena kwa iye ndi mnyamata wace, Munanka kuti? Ndipo iye anati, Kukafuna aburuwo; ndipo pakuona kuti sitinawapeza, tinadza kwa Samueli.

15. Ndipo mbale wa atate wa Sauli anati, Undiuze cimene Samueli analankhula nawe.

16. Ndipo Sauli anati kwa mbale wa atate wace, Anatiuza momveka kuti aburuwo anapezedwa kale. Koma sanamdziwitsa mau aja Samueli ananena zaufumuwo.

17. Ndipo Samueli anaitana anthu onse asonkhane kwa Yehova ku Mizipa;

18. nanena ndi ana a Israyeli, Atero Yehova, Mulungu wa Israyeli kuti, Ine ndinaturutsa Israyeli m'Aigupto, ndipo ndinakupulumutsani m'manja a Aaigupto, ndi m'manja a maufumu onse anakusautsani;

19. koma lero inu mwakana Mulungu wanu amene anakupulumutsani yekha m'matsoka anu onse, ndi m'masautso anu; ndipo munanena naye, Koma mutipatse mfumu. Cifukwa cace tsono mudzionetse pamaso pa Mulungu mafuko mafuko, ndi magulu magulu.

20. Comweco Samueli anayandikizitsa mafuko onse a Israyeli, ndipo pfuko la Benjamini linasankhidwa.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 10