Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 10:4-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Iwowa adzakulankhulani, ndi kukupatsani mikate iwiri; imeneyi mudzailandira m'manja mwao.

5. Ndipo m'tsogolo mwace mudzafika ku phiri la Mulungu, kumene kuli kaboma ka Afilisti; ndipo kudzali kuti pakufika inu kumudziko mudzakomana ndi gulu la aneneri, alikutsika kumsanje ndi cisakasa, ndi lingaka, ndi toliro, ndi zeze, pamaso pao; iwo adzanenera;

6. ndipo Mzimu wa Yehova udzagwera inu kolimba, nanunso mudzanenera pamodzi nao, nimudzasandulika munthu wina.

7. Ndipo zitakufikirani zizindikilo izi mudzacita monga mudzaona pocita, pakuti Mulungu ali nanu.

8. Ndipo mudzatsika patsogolo pa ine kunka ku Giligala; ndipo, taonani, ndidzatsikira kwa inu kukapereka zopsereza, ndi kuphera nsembe zamtendere. Mutsotsepo masiku asanu ndi awiri kufikira ndikatsikira kwa inu ndi kukudziwitsani cimene mudzacita.

9. Ndipo kunali, pamene iye anapotoloka kuti alekane ndi Samueli, Mulungu anampatsa mtima wina watsopano; ndipo zizindikilo zija zonse zinacitika tsiku lija.

10. Ndipo pamene anafika kucitunda kuja, onani, gulu la aneneri linakomana naye; ndi Mzimu wa Mulungu unamgwera mwamphamvu, iye nanenera pakati pao,

11. Ndipo kunali, kuti onse amene anamdziwiratu kale, pakuona ici cakuti, onani, iye ananenera pamodzi ndi aneneri, anati wina ndi mnzace, Ici nciani cinamgwera mwana wa Kisi? Kodi Saulinso ali mwa aneneri?

12. Ndipo munthu wina wa komweko anayankha nati, Ndipo atate wao ndiye yani? Cifukwa cace mauwa anakhala ngati mwambi, Kodi Saulinso ali mwa aneneri?

13. Ndipo pamene adatha kunenera anafika kumsanjeko.

14. Ndipo mbale wa atate wace wa Sauli ananena kwa iye ndi mnyamata wace, Munanka kuti? Ndipo iye anati, Kukafuna aburuwo; ndipo pakuona kuti sitinawapeza, tinadza kwa Samueli.

15. Ndipo mbale wa atate wa Sauli anati, Undiuze cimene Samueli analankhula nawe.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 10