Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 8:1-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo Solomo anasonkhanitsa akulu a Israyeli, ndi akulu onse a mafuko, akalonga a nyumba za atate a ana a Israyeli, kwa mfumu Solomo m'Yerusalemu, kukatenga likasa la cipangano ca Yehova m'mudzi wa Davide, ndiwo Ziyoni.

2. Ndipo anthu onse a Israyeli anasonkhana kwa mfumu Solomo kukadyereram'mwezi wa Etanimu, ndiwo mwezi wacisanu ndi ciwiri.

3. Ndipo akulu onse a Israyeli anadza, ansembe nanyamula likasa.

4. Ndipo anatenga likasa la Yehova, ndi cihema cokomanako, ndi zipangizo zonse zopatulika, zinali m'cihemamo, inde zimenezi anazitenga ansembe ndi Alevi.

5. Ndipo mfumu Solomo ndi msonkhano wonse wa Israyeli wosonkhana kwa iye anali naye kulikasa, naphera nkhosa ndi ng'ombe za nsembe zosawerengeka ndi zosadziwika, cifukwa ca unyinji wao.

6. Ndipo ansembe analonga likasa la cipangano ca Yehova kumalo kwace, ku monenera mwa nyumba, ku malo opatulikitsa, munsi mwa mapiko a akerubi,

7. Popeza akerubiwo anatambasula mapiko ao awiri pamwamba pa likasa, ndipo akerubiwo anaphimba pamwamba pa likasa ndi mphiko zace.

8. Ndipo mphikozo zinatalika kuti nsonga za mphiko zidaoneka ku malo opatulika cakuno ca monenera; koma sizinaoneka kubwalo; ndipo zikhala pomwepo mpaka lero lino.

9. Munalibe kanthu m'likasamo koma magome awiri aja amwala Mose anawalongamo pa Horebu, pamene Yehova anapangana ndi ana a Israyeli, poturuka iwo m'dziko la Aigupto.

10. Ndipo kunacitika ataturuka ansembe m'malo opatulika, mtambo unadzaza nyumba ya Yehova,

11. ndipo ansembe sanakhoza kuimirira kurumikira cifukwa ca mtambowo, popeza ulemerero wa Yehova unadzazanyumba ya Yehova.

12. Pamenepo Solomo anati, Yehova ananena kuti adzakhala m'mdima waukuru.

13. Ine ndakumangirani ndithu nyumba yokhalamo Inu, ndiyo malo okhalamo inu nthawi zosatha.

14. Ndipo mfumu inapotoloka nkhope yace, nidalitsa msonkhano wonse wa Israyeli, Ndi msonkhano wonse wa Israyeli unaimirira.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 8