Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 7:29-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Ndipo pa matsekerezo a pakati pa mbano panali ngati mikango ndi ng'ombe ndi akerubi, ndi pamwamba pa mbano panali cosanjikirapo; ndipo pansi pa mikango ndi ng'ombe panaphatikizika zotsetseremba zoyangayanga zokoloweka.

30. Ndipo phaka lid lonse linali ndi njinga zamkuwa zinai ndi mitanda yamkuwa, ndipo ngondya zace zinai zinali ndi mapewa; pansi pa thawale panali mapewa oyengeka pa mbali pa zophatikizika zonse.

31. Ndipo pakamwa pace m'katimo pamwamba pa cosanjikira, panayesa mkono umodzi; koma pakamwa pace panali posadamuka, monga mapangidwe ace a cosanjikira, mkono umodzi ndi nusu; ndiponso pakamwa pace panali zolemba ndi matsekerezo ace anali amphwamphwa, si ozunguniza.

32. Ndipo njinga zinai zinali pansi pa matsekerezo, ndi mitanda ya njinga inali m'mphakamo, ndi msinkhu wa njinga imodzi unali mkono umodzi ndi nusu.

33. Ndipo mapangidwe a njinga analingana ndi mapangidwe a njinga za gareta, mitanda yace ndi mkombero wace ndi nthiti zace ndi mtima wace zonsezo zinayengedwa.

34. Ndipo panali ngati mapewa anai pansi pa ngondya zinai za phaka limodzi, mapewawo anali a phaka lomwelo.

35. Ndipo pamwamba pa phaka panali khoma lozunguniza, msinkhu wace nusu ya mkono; ndi pamwamba pa phaka panali mbano zace ndi matsekerezo a phaka lomwelo.

36. Ndipo m'mapanthi mwa mbano zace ndi pa matsekerezo ace analemba ngati akerubi ndi mikango ndi migwalangwa, monga mwa malo ace a zonsezo, ndi zoyangayanga zozungulira.

37. Motero anapanga maphaka khumiwo, anafanana mayengedwe ao muyeso wao ndi maonekedwe ao.

38. Ndipo anapanga mbiya zamphwamphwa khumi zamkuwa; m'mbiya imodziyo munalowamo madzi a mitsuko yaikuru makumi anai, ndipo mbiya iri yonse inali ya mikono inai: pa phaka liri lonse la maphaka aja khumi panakhala mbiya imodzi.

39. Ndipo anaika maphaka asanu ku dzanja lamanja la nyumba, ndi maphaka asanu ku dzanja lamanzere la nyumba; naika thawalelo ku dzanja lamanja la nyumba kum'mawa kupenya kumwera.

40. Ndipo Hiramu anayenga mbiyazo ndi zoolera ndi mbale zowazira. Motero Hiramu anatsiriza kupanga nchito yonse anaicitira mfumu Solomo ya m'nyumba ya Yehova.

41. Nsanamira ziwirizo, ndi mbale za mitu inali pamwamba pa nsanamira ziwirizo, ndi maukonde awiri ophimbira mbale ziwiri za mitu inali pamwamba pa nsanamirazo,

42. ndi makangaza mazana anai a maukonde awiriwo, mizere iwiri ya makangaza a ukonde umodzi kuphimbira mbale ziwiri za mitu inali pa nsanamirazo,

43. ndi maphaka khumiwo ndi mbiya khumi ziri pa maphakawo,

44. ndi thawale limodzilo, ndi ng'ombe khumi mphambu ziwirizo pansi pa thawale;

45. ndi miphikayo, ndi zoolerazo, ndi mbalezo; inde zotengera zonse zimene Hiramu anampangira mfumu Solomo za m'nyumba ya Yehova, zinali za mkuwa wonyezimira.

46. Mfumu inaziyenga pa cidikha ca ku Yordano, m'dothe ladongo, pauti pa Sukoti ndi Zaritani.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 7