Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 6:7-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo nyumbayo pomangidwa inamangidwa ndi miyala yokonzeratu asanaitute; ndipo m'nyumbamo simunamveka: kulira nyundo, kapena nkhwangwa, kapena cipangizo cacitsulo, pomangidwa iyo.

8. Khomo lolowera m'zipinda za pakati linali ku mbali ya ku dzanja lamanja ya nyumba; ndipo anthu amakwerera pa makwerero ozunguniza, kutikira ku zipinda za pakati, ndi kuturuka m'zapakatizo kulowa m'zacitatuzo,

9. Momwemo anamanga nyumbayo naitsiriza, naika mitanda, naifolera ndi matabwa amikungudza.

10. Ndipo anamanga zipindazo zogundana ndi nyumba yonseyo, cipinda ciri conse msinkhu wace mikono isanu; ndipo anazilumikizitsa kunyumba ndi mitengo yamkungudza.

11. Ndipo mau a Yehova anafika kwa Solomo, nati,

12. Kunena za nyumba yino ulikuimanga, ukamayenda iwe m'malemba anga, ndi kumacita maweruzo anga, ndi kumasunga malamulo anga onse kuyendamo, pamenepo Ine ndidzakhazikitsira iwe mau anga amene ndinauza Davide atate wako.

13. Ndipo ndidzakhala pakati pa ana a Israyeli osawasiya anthu anga a Israyeli.

14. Tsono Solomo anamanga nyumbayo naitsiriza.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 6