Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 19:7-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo mthenga wa Yehova anafikanso kaciwiri, namkhudza, nati, Tauka, idya, popeza ulendo udzakulaka.

8. Tsono anauka, nadya namwa, nayenda ndi mphamvuya cakudya cimeneco masiku makumi anai usana ndi usiku, nafika ku phiri la Mulungu ku Horebu.

9. Nafika kuphanga, nagona kumeneko, ndipo taonani, mau a Yehova anamfikira, nati kwa iye, Ucitanji pano, Eliya?

10. Ndipo anati, Ine ndinacitira cangu Yehova Mulungu wa makamu; popeza ana a Israyeli anasiya cipangano canu, napasula maguwa anu a nsembe, napha aneneri anu ndi lupanga, ndipo ndatsala ndekha, ndipo afuna moyo wanga kuucotsa.

11. Ndipo iye anati, Turuka, nuime pa phiri tino pamaso pa Yehova. Ndipo taonani, Yehova anapitapo, ndi mphepo yaikuru ndi yamphamvu inang'amba mapiri, niphwanya matanthwe pamaso pa Yehova; koma Yehova sanakhala m'mphepomo. Itapita mphepoyo kunali cibvomezi; komanso Yehova sanali m'cibvomezico.

12. Citaleka cibvomezi panali moto; koma Yehova sanali m'motomo, Utaleka mota panali bata la kamphepo kayaziyazi.

13. Ndipo atamva Eliya, anapfunda nkhope yace ndi copfunda cace, naturuka, naima pa khomo la phangalo. Ndipo taonani, anamdzera mau akunena naye, Ucitanji kuno, Eliya?

14. Nati iye, Ndacitira cangu Yehova Mulungu wa makamu; popeza ana a Israyeli ataya cipangano canu, nagumula maguwa a nsembe anu, napha aneneri anu ndi lupanga; ndipo ndatsala ndekha, ndipo afuna moyo wanga kuucotsa.

15. Ndipo Yehova anati kwa iye, Bwerera ulendo wako, udzere kucipululu kumka ku Damasiko, ndipo utafikako udzoze Hazaeli akhale mfumu ya Aramu;

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 19