Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 21:9-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo pamene anaturukira pamtunda, anapenya moto wamakara pomwepo, ndi kansomba kosanjikikako, ndi mkate.

10. Yesu ananena nao, Tenganiko nsomba zimene mwazigwira tsopano,

11. Cifukwa cace Simoni Petro anakwera m'ngalawa nakokera khoka kumtunda Iodzala ndi nsomba zazikuru, zana limodzi, ndi makumiasanu ndi zitatu; ndipo zingakhale zinacuruka kotere, kokha silinang'ambika.

12. Yesu ananena nao, Idzani mufisule. Koma palibe mmodzi wa akuphunzira anatha kumfunsa iye, Ndinu yani? podziwa kuti ndiye Ambuye.

13. Yesu anadza natenga mkate napatsa Iwo, momwemonso nsomba.

14. Imeneyo ndi nthawi yacitatu yakudzionetsera Yesu kwa akuphunzira ace, m'mene atauka kwa akufa.

15. Ndipo pamene atafisula Yesu ananena kwa Simoni Petro, Simoni mwana wa Yona, kodi undikonda Ine koposa awa? Ananena ndi iye, Inde, Ambuye; mudziwa kuti ndikukondani Inu. Ananena naye, Dyetsa ana a nkhosa anga.

16. Ananena nayenso kaciwiri, Simoni mwana wa Yona, ukonda Ine kodi? Ananena ndi iye, Inde, Ambuye; mudziwa kuti ndikukondani Inu. Ananena naye, Weta nkhosa zanga.

17. Ananena: naye kacitatu, Simoni mwana wa Yona, kodi undikonda Ine? Petro anamva cisoni kuti anati kwa iye kacitatu, Kodi undikonda Ine? ndipo anati kwa iye, Ambuye, mudziwa Inu zonse; muzindikira kuti ndikukondani Inu. Yesu ananena naye, Dyetsa nkhosa zanga.

18. Indetu, indetu, ndinena ndi iwe, pamene unali mnyamata unadzimangira wekha m'cuuno, ndipo unayenda kumene unafuna; koma pamene udzakalamba udzaturutsa manja ako, ndipo adzakumanga wina, nadzakunyamula kumene sufuna.

19. Koma ici ananena ndi kuzindikiritsa imfa imene adzalemekeza nayo Mulungu. Ndipo m'mene ananena ici, anati kwa iye, nditsate Ine,

20. Petro, m'mene anaceuka, anapenya wophunzira amene Yesu anamkonda alikutsata, amenenso anatsamira pacifuwa pace pamgonero, nati, Ambuye, ndani iye wakupereka Inu?

21. Pamenepo Petro pakumuona, ananena kwa Yesu, Ambuye, koma nanga uyu?

Werengani mutu wathunthu Yohane 21