Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 9:8-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. koma ena, kuti Eliya anaoneka; ndipo ena, kuti mneneri wina wa akale aja anauka.

9. Ndipo Herode anati, Yohane ndinamdula mutu ine; koma uyu ndani ndikumva zotere za iye? Ndipo anafunafuna kumuona iye.

10. Ndipo atabwera atumwi, anamfotokozera iye zonse anazicita. Ndipo iye anawatenga, napatuka nao pa okha kunka ku mudzi dzina lace Betsaida.

11. Koma unyinji wa anthu, pamene anadziwa, anamtsata Iye; ndipo iye anawalandira, nalankhula nao za Ufumu wa Mulungu, naciritsa amene anasowa kuciritsidwa.

12. Koma dzuwa lidapendeka; ndipo khumi ndi awiriwo anadza, nati kwa iye, Tauzani makamu a anthu amuke, kuti apite ku midzi yoyandikira ndi kumiraga, kukafuna pogona, ndi kupeza zakudya; cifukwa tiri ku malo acipululu kuno.

13. Koma anati kwa iwo, Muwapatse kudya ndinu. Koma anati, Ife tiribe mikate, koma isanu yokha, ndi nsomba ziwiri zokha; kapena timuke ife kukagulira anthu awa onse zakudya.

14. Pakuti anali amuna ngati zikwi zisanu. Koma iye anati kwa ophunzira ace, Khalitsani iwo pansi magulu magulu, ngati makumi asanu asanu.

15. Ndipo anatero, nawakhalitsa pansi onsewo.

16. Ndipo iye, m'mene anatenga mikate isanu ija ndi nsomba ziwiri anayang'ana kumwamba, nazidalitsa, nanyema, napatsa ophunzira apereke kwa anthuwo.

17. Ndipo anadya, nakhuta onsewo; natola makombo, mitanga khumi ndi iwiri.

18. Ndipo kunali, pamene iye analikupemphera padera, ophunzira anali naye; ndipo anawafunsa iwo, kuti, Makamuwo a anthu anena kuti Ine ndine yani?

19. Ndipo anayankha nati, Yohane Mbatizi; koma ena, Eliya; ndi ena, kuti anauka mmodzi wa aneneri akale.

20. Ndipo anati kwa iwo, Koma inu munena kuti Ine ndine yani? Ndipo anayankha Petro, nati, Kristu wa Mulungu.

Werengani mutu wathunthu Luka 9