Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 5:12-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo panali, pamene iye anali m'mudzi wina, taona, munthu wodzala ndikhate; ndipopameneanaona Yesu, anagwa nkhope yace pansi, nampempha iye, nanena, Ambuye, ngati mufuna mungathe kundikonza.

13. Ndipo iye anatambalitsa dzanja lace, namkhudza, nanena, Ndifuna, takonzeka, Ndipo pomwepo khate linacoka kwa iye.

14. Ndipo iye anamuuzitsa, kuti asanene kwa munthu ali yense; koma ucoke, nudzionetse wekha kwa wansembe, nupereke nsembe ya pa cikonzedwe cako, monga adalamulira Mose, kukhale umboni kwa iwo.

15. Koma makamaka mbiri yace ya iye inabuka: ndipo mipingo yambiri ya anthu inasonkhanakudzamvera, ndi kudzaciritsidwa nthenda zao.

16. Koma iye anazemba, nanka m'mapululu, nalikupemphera.

17. Ndipo panali tsiku limodzi la masiku awo, iye analikuphunzitsa; ndipo analikukhalapo Afarisi ndi aphunzitsi a malamulo, amene anacokera ku midzi yonse ya ku Galileya, ndi Yudeya ndi Yerusalemu: ndipo mphamvu ya Ambuye inali ndi iye yakuwaciritsa,

18. Ndipo onani, anthu alikunyamulira pakama munthu wamanjenje; nafunafuna kulowa naye, ndi kumuika pamaso pa iye.

19. Ndipo posapeza polowa naye, cifukwa ca unyinji wa anthu, anakwera pamwamba pa chindwi, namtsitsira iye poboola pa chindwi ndi kama wace, namfikitsa pakati pomwe pamaso pa Yesu.

20. Ndipo iye, pakuona cikhulupiriro cao, anati, Munthu iwe, macimo ako akhululukidwa.

21. Ndipo alembi ndi Afarisi anayamba kuyesayesa mumtima mwao, kuti, ndani Uyu alankhula zomcitira Mulungu mwano? Ndani angathe kukhululukira macimo, koma Mulungu yekha?

22. Koma Yesu anadziwa zoyesayesa zao, nayankha, nati kwa iwo, Muyesayesa bwanji m'mitima yanu?

23. Capafupi nciti, kunena, Akhululukidwa kwa iwe macimo ako; kapena kunena, Tauka, nuyende?

Werengani mutu wathunthu Luka 5