Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 4:28-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Ndipo onse a m'sunagogemo anadzala ndi mkwiyo pakumva izi;

29. nanyamuka na mturutsira Iye kunja kwa mudziwo, nanka naye pamutu pa phiri pamene panamangidwa mudzi wao, kuti akamponye iye pansi.

30. Koma iye anapyola pakati pao, nacokapo.

31. Ndipo iye anatsika nadza ku Kapernao, ndiwo mudzi wa ku Galileya, Ndipo analikuwaphunzitsa iwo pa Sabata; ndipo anadabwa ndi ciphunzitso cace;

32. cifukwa mau ace anali ndi ulamuliro.

33. Ndipo munali m'sunagoge munthu, wokhala naco ciwanda conyansa; napfuula ndi mau olimba, kuti,

34. Ha! tiri ndi ciani ndi Inu, Yesu wa ku N azarete? kodi munadza kutiononga ife? ndikudziwani Inu muli yani, ndinu Woyera wace wa Mulungu.

35. Ndipo Yesu anamdzudzula iye, nanena, Tonthola, nuturuke mwa iye. Ndipo ciwandaco m'mene cinamgwetsa iye pakati, cinaturuka mwa iye cosampweteka konse.

36. Ndipo anthu onse anadabwa, nalankhulana wina ndi mnzace, nanena, Mau amenewa ali otani? cifukwa ndi ulamuliro ndi mphamvu angolamulira mizimu yonyansa, ndipo ingoturuka.

37. Ndipo mbiri yace ya iye inafalikira ku malo onse a dziko Ioyandikira.

38. Ndipo iye ananyamuka kucokera m'sunagoge, nalowa m'nyumba ya Simoni. Koma momwemo munali mpongozi wace wa Simoni, anagwidwa ndi nthenda yolimba yamalungo; ndipo anampempha Yesu za iye.

39. Ndipo iye anaimirira, naweramira pa iye, nadzudzula nthendayo; ndipo inamleka iye: ndipo anauka msangatu, nawatumikira.

40. Ndipo pakulowa dzuwa anthu onse amene anali nao odwala ndi nthenda za mitundu mitundu, anadza nao kwa iye; ndipo iye anaika manja ace pa munthu ali yense wa iwo, nawaciritsa.

41. Ndi ziwanda zomwe zinaturuka mwa ambiri, ndi kupfuula, kuti, Inu ndinu Mwana wa Mulungu. Ndipo iye anazidzudzula, wosazilola kulankhula, cifukwa zinamdziwa kuti iye ndiye Kristu.

42. Ndipo kutaca anaturuka iye nanka ku malo acipululu; ndi makamu a anthu analikwnfunafuna iye, nadza nafika kwa iye, nayesa kumletsa iye, kuti asawacokere.

43. Koma anati kwa iwo, Kundiyenera Ine ndilalikire Uthenga Wabwino wa Ufumu wa Mulungu ku midzi yinanso: cifukwa ndinatumidwa kudzatero.

Werengani mutu wathunthu Luka 4