Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Luka 11:25-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. ndipo pofika, uipeza yosesa ndi yokonzeka.

26. Pomwepo, upita nutenga mizimu yina isanu ndi iwiri yoipa yoposa ndi uwu mwini; ndipo ilowa nikhalira komweko; ndipo makhalidwe otsiriza a munthu uyu aipa koposa oyambawo.

27. Ndipo kunali, pakunena izi iye, mkazi wina mwa khamu la anthu anakweza mau, nati kwa iye, Yodala mimba imene idakubalani, ndi mawere amene munayamwa.

28. Koma iye anati, Inde, koma odala iwo akumva mau a Mulungu, nawasunga.

29. Ndipo pakusonkhana pamodzi makamu a anthu, anayamba kunena, Mbadwo uno ndi mbadwo woipa; ufuna cizindikilo, ndipo cizindikilo sicidzapatsidwa kwa uwu koma cizindikilo ca Yona.

30. Pakuti monga ngati Yona anali cizindikilo kwa Anineve, cotero adzakhalanso Mwana wa munthu kwa mbadwo uno.

31. Mfumu yaikazi ya kumwera idzaimirira pa mlandu wotsiriza pamodzi ndi amuna a mbadwo uno, nadzawatsutsa; pakuti anadza ku'cokera ku malekezero a dziko kudzamva nzeru za Solomo; ndipo onani, woposa Solomo ali pano.

Werengani mutu wathunthu Luka 11